< Song of Solomon 1 >

1 The Song of songs, which is Solomon's.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Let him kiss me with the kisses of his mouth; for your love is better than wine.
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Your oils have a pleasing fragrance. Your name is oil poured forth, therefore the virgins love you.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Take me away with you. Let us hurry. The king has brought me into his chambers. We will be glad and rejoice in you. We will praise your love more than wine. They are right to love you.
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 I am dark, but lovely, you daughters of Jerusalem, like Kedar's tents, like Solomon's curtains.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Do not stare at me because I am dark, because the sun has scorched me. My mother's sons were angry with me. They made me keeper of the vineyards. I haven't kept my own vineyard.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Tell me, you whom my soul loves, where you graze your flock, where you rest them at noon; For why should I be as one who is veiled beside the flocks of your companions?
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 If you do not know, most beautiful among women, follow the tracks of the sheep. Graze your young goats beside the shepherds' tents.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 I have compared you, my love, to a steed in Pharaoh's chariots.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Your cheeks are beautiful with earrings, your neck with strings of jewels.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 We will make you earrings of gold, with studs of silver.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 While the king sat at his table, my perfume spread its fragrance.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 My beloved is to me a sachet of myrrh, that lies between my breasts.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 My beloved is to me a cluster of henna blossoms from the vineyards of En Gedi.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 Look, you are beautiful, my love. Look, you are beautiful. Your eyes are doves.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 Look, you are beautiful, my beloved, yes, pleasant; and our couch is verdant.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 The beams of our house are cedars. Our rafters are firs.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.

< Song of Solomon 1 >