< Mark 1 >

1 The beginning of the Good News of Yeshua Meshikha, the Son of God.
Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
2 As it is written in Eshaya the prophet, "Look, I send my messenger ahead of you, who will prepare your way before you.
monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
3 The voice of one crying in the wilderness, 'Prepare the way of the Lord. Make his roads straight.'"
“Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
4 Yukhanan came baptizing in the wilderness and preaching a baptism of repentance for forgiveness of sins.
Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
5 And all the country of Yehuda went out to him and all those from Urishlim, and they were baptized by him in the Yurdinan river, confessing their sins.
Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
6 And Yukhanan was clothed with camel's hair and a leather belt around his waist. He ate locusts and wild honey.
Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
7 And he preached, saying, "After me comes he who is mightier than I, the strap of whose sandals I am not worthy to stoop down and loosen.
Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
8 I baptized you in water, but he will baptize you in the Rukha d'Qudsha."
Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
9 And it happened in those days, that Yeshua came from Natsrath of Galila, and was baptized by Yukhanan in the Yurdinan.
Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
10 And immediately coming up from the water, he saw the heavens parting, and the Rukha descending on him like a dove.
Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
11 And a voice came out of the sky, "You are my beloved Son, with you I am well pleased."
Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
12 And immediately the Rukha drove him out into the wilderness.
Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
13 And he was in the wilderness forty days tempted by Satana. He was with the wild animals; and the angels were serving him.
ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
14 Now after Yukhanan was taken into custody, Yeshua came into Galila, proclaiming the Good News of God,
Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
15 and saying, "The time is fulfilled, and the Kingdom of God is near. Repent, and believe in the Good News."
“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
16 And passing along by the lake of Galila, he saw Shimon and Andreus the brother of Shimon casting a net into the lake, for they were fishermen.
Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
17 And Yeshua said to them, "Come, follow me, and I will make you into fishers of people."
Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
18 And immediately they left the nets, and followed him.
Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
19 And going on a little further, he saw Yaquv the son of Zabedai, and Yukhanan, his brother, who were also in the boat mending the nets.
Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
20 And immediately he called them, and they left their father, Zabedai, in the boat with the hired servants, and went after him.
Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
21 And they went into Kepharnakhum, and immediately on the Sabbath day he entered into the synagogue and taught.
Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
22 And they were astonished at his teaching, for he taught them as having authority, and not as the scribes.
Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
23 And just then there was in their synagogue a man with an unclean spirit, and he shouted,
Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
24 saying, "What do we have to do with you, Yeshua, Natsraya? Have you come to destroy us? I know you who you are: the Holy One of God."
“Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
25 And Yeshua rebuked him, saying, "Be quiet, and come out of him."
Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
26 And the unclean spirit, convulsing him and crying with a loud voice, came out of him.
Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
27 And they were all amazed, so that they questioned among themselves, saying, "What is this? A new teaching? For with authority he commands even the unclean spirits, and they obey him."
Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
28 And at once the news of him went out everywhere into all the region of Galila and its surrounding area.
Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
29 And immediately, when they had come out of the synagogue, they came into the house of Shimon and Andreus, with Yaquv and Yukhanan.
Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
30 Now Shimon's mother-in-law was sick in bed with a fever, and immediately they told him about her.
Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
31 And he came and took her by the hand, and raised her up. The fever left her, and she served them.
Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
32 At evening, when the sun had set, they brought to him all who were sick, and those who were possessed by demons.
Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
33 And all the city was gathered together at the door.
Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
34 And he healed many who were sick with various diseases, and cast out many demons. He did not allow the demons to speak, because they knew him.
Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
35 And early in the morning, while it was still dark, he rose up and went out, and departed into a deserted place, and prayed there.
Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
36 And Shimon and those who were with him followed after him;
Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
37 and they found him, and told him, "Everyone is looking for you."
ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
38 And he said to them, "Let us go somewhere else into the next towns, that I may preach there also, because I came out for this reason."
Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
39 And he went into their synagogues throughout all Galila, preaching and casting out demons.
Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
40 And a leper came to him, begging him, and knelt down and said to him, "Lord, if you want to, you can make me clean."
Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
41 And being moved with compassion, he stretched out his hand, and touched him, and said to him, "I am willing. Be cleansed."
Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
42 And immediately the leprosy departed from him, and he was made clean.
Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
43 And he strictly warned him, and immediately sent him out,
Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
44 and said to him, "See you say nothing to anyone, but go show yourself to the priest, and offer for your cleansing the things which Mushe commanded, for a testimony to them."
“Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
45 But he went out, and began to proclaim it freely, and to spread about the matter, so that Yeshua could no more openly enter into a city, but was outside in desert places: and they came to him from everywhere.
Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.

< Mark 1 >