< John 1 >

1 In the beginning was the Word, and the Word was with God, and the Word was God.
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 He was in the beginning with God.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 All things were made through him, and apart from him nothing was made that has been made.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 In him was life, and the life was the light of humanity.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 And the light shines in the darkness, and the darkness hasn't overcome it.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 There came a man, sent from God, whose name was Yukhanan.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 He came as a witness to testify about the light, that all might believe through him.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 He was not the light, but was sent that he might testify about the light.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 The true light that enlightens everyone was coming into the world.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 He was in the world, and the world was made through him, but the world did not recognize him.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 He came to his own, and those who were his own did not receive him.
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 But as many as received him, to them he gave the right to become God's children, to those who believe in his name,
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 who were born not of blood, nor of the will of the flesh, nor of the will of man, but of God.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 And the Word became flesh and lived among us, and we saw his glory, such glory as of the one and only of the Father, full of grace and truth.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 Yukhanan testified about him. He shouted out, saying, "This was the one of whom I said, 'He who comes after me has surpassed me, for he was before me.'"
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 For of his fullness we all received, and grace upon grace.
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 For the Law was given through Mushe, grace and truth came through Yeshua Meshikha.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 No one has seen God at any time. The only Son, who is at the Father's side, has made him known.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 And this is Yukhanan's testimony, when the Jewish leaders sent priests and Levites from Urishlim to ask him, "Who are you?"
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 And he confessed, and did not deny, but he confessed, "I am not the Meshikha."
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 And they asked him, "What then? Are you Eliya?" And he said, "I am not." "Are you the Prophet?" And he answered, "No."
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 They said therefore to him, "Who are you? Give us an answer to take back to those who sent us. What do you say about yourself?"
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 He said, "I am the voice of one crying in the wilderness, 'Make straight the way of the Lord,' as Eshaya the prophet said."
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 (Now they had been sent from the Pharisees.)
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 And they asked him, "Why then do you baptize, if you are not the Meshikha, nor Eliya, nor the Prophet?"
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 Yukhanan answered them, saying, "I baptize in water, but among you stands one whom you do not know.
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 He is the one who comes after me, whose sandal strap I'm not worthy to loosen."
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 These things were done in Beth-Naiya across the Yurdinan, where Yukhanan was baptizing.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 The next day, he saw Yeshua coming to him, and said, "Look, the Lamb of God, who takes away the sin of the world.
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 This is he of whom I said, 'After me comes a man who ranks ahead of me, because he existed before me.'
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 I did not know him, but for this reason I came baptizing in water: that he would be revealed to Israyel."
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 And Yukhanan testified, saying, "I saw the Rukha descending like a dove out of heaven, and it remained on him.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 And I did not recognize him, but he who sent me to baptize in water, he said to me, 'On whomever you will see the Rukha descending, and remaining on him, this is he who baptizes in the Rukha d'Qudsha.'
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 And I have seen and have testified that this is the Chosen One of God."
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 Again, the next day, Yukhanan was standing with two of his disciples,
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 and he looked at Yeshua as he walked, and said, "Look, the Lamb of God."
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 And the two disciples heard him say this, and they followed Yeshua.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 And Yeshua turned and saw them following, and said to them, "What are you looking for?" They said to him, "Rabbi" (which translated means Teacher), "where are you staying?"
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 He said to them, "Come, and you will see." They came and saw where he was staying, and they stayed with him that day. It was about four in the afternoon.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 One of the two who heard Yukhanan, and followed him, was Andreus, Shimon Kipha's brother.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 He first found his own brother, Shimon, and said to him, "We have found the Meshikha." (which is translated, Anointed One).
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 He brought him to Yeshua. Yeshua looked at him, and said, "You are Shimon the son of Yukhanan. You shall be called Kipha" (which is translated, rock).
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 On the next day, he was determined to go out into Galila, and he found Philipus. And Yeshua said to him, "Follow me."
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 Now Philipus was from Beth-Sayada, of the city of Andreus and Kipha.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 Philipus found Nathanayil, and said to him, "We have found him of whom Mushe in the Law and the Prophets wrote: Yeshua of Natsrath, the son of Yauseph."
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 And Nathanayil said to him, "Can any good thing come out of Natsrath?" Philipus said to him, "Come and see."
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 Yeshua saw Nathanayil coming to him, and said about him, "Look, a true Israyelite in whom there is no deceit."
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 Nathanayil said to him, "How do you know me?" Yeshua answered him, "Before Philipus called you, when you were under the fig tree, I saw you."
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 Nathanayil answered him, "Rabbi, you are the Son of God. You are King of Israyel."
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 Yeshua answered him, "Because I told you, 'I saw you underneath the fig tree,' do you believe? You will see greater things than these."
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 And he said to him, "Truly, truly, I tell you, you will see heaven opened, and the angels of God ascending and descending on the Son of Man."
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

< John 1 >