< Genesis 16 >

1 Now Sarai, Abram's wife, bore him no children, but she had an Egyptian servant whose name was Hagar.
Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara;
2 Sarai said to Abram, "Look now, God has prevented me from bearing. Please go in to my servant. It may be that I will obtain children by her." Abram listened to the voice of Sarai.
ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.” Abramu anamvera Sarai.
3 So Sarai, Abram's wife, took Hagar the Egyptian, her servant, after Abram had lived ten years in the land of Canaan, and gave her to Abram her husband to be his wife.
Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi.
4 He slept with Hagar, and she conceived. When she saw that she had conceived, her mistress was despised in her eyes.
Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba. Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai.
5 Sarai said to Abram, "This wrong is your fault. I gave my servant into your bosom, and when she saw that she had conceived, she despised me. God judge between me and you."
Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”
6 But Abram said to Sarai, "Look, your servant is in your hand. Do to her whatever is good in your sight." Sarai dealt harshly with her, so she fled from her presence.
Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.
7 And the angel of God found her by a spring of water in the desert, by the spring on the way to Shur.
Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri.
8 And he said, "Hagar, servant of Sarai, where did you come from, and where are you going?" And she said, "I am running away from the presence of my mistress Sarai."
Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”
9 The angel of the LORD said to her, "Return to your mistress, and submit yourself to her authority."
Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere.
10 The angel of the LORD said to her, "I will greatly multiply your descendants, so that they will be too numerous to count."
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”
11 Then the angel of God said to her, "Look, you are with child, and will bear a son. You are to name him Ishmael, because God has heard your affliction.
Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti, “Ndiwe woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna. Udzamutcha dzina lake Ismaeli, pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
12 He will be like a wild donkey among men. His hand will be against every man, and every man's hand against him. And he will live away from all of his brothers."
Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala; adzadana ndi aliyense ndipo anthu onse adzadana naye, adzakhala mwaudani pakati pa abale ake onse.”
13 And she called his name, the one who spoke to her, "You are El Roi," for she said, "Here I have seen the one who sees me."
Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.”
14 Therefore the well was called Beer Lahai Roi. Look, it is between Kadesh and Bered.
Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.
15 Hagar bore a son for Abram. Abram called the name of his son, whom Hagar bore, Ishmael.
Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli.
16 Abram was eighty-six years old when Hagar bore Ishmael to Abram.
Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

< Genesis 16 >