< Ezekiel 25 >

1 The word of the LORD came to me, saying,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 "Son of man, set your face toward the people of Ammon, and prophesy against them:
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
3 and tell the people of Ammon, 'Hear the word of the LORD: Thus says the LORD, "Because you said, 'Aha,' against my sanctuary, when it was profaned; and against the land of Israel, when it was made desolate; and against the house of Judah, when they went into captivity:
Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
4 therefore, look, I will deliver you to the people of the east for a possession, and they shall set their encampments in you, and make their dwellings in you; they shall eat your fruit, and they shall drink your milk.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
5 I will make Rabbah a stable for camels, and the people of Ammon a resting place for flocks: and you shall know that I am the LORD."
Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 For thus says the LORD: "Because you have clapped your hands, and stamped with the feet, and rejoiced with all the despite of your soul against the land of Israel;
Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
7 therefore, look, I have stretched out my hand on you, and will deliver you for a spoil to the nations; and I will cut you off from the peoples, and I will cause you to perish out of the countries: I will destroy you; and you shall know that I am the LORD."'"
Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
8 "Thus says the LORD: 'Because Moab and Seir say, "Look, the house of Judah is like all the nations";
“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
9 therefore, look, I will open the side of Moab from the cities, from his cities which are on his frontiers, the glory of the country, Beth Jeshimoth, Baal Meon, and Kiriathaim,
Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
10 to the people of the east, to go against the people of Ammon; and I will give them for a possession, that the people of Ammon may not be remembered among the nations.
Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
11 and I will execute judgments on Moab; and they shall know that I am the LORD.'"
Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
12 "Thus says the LORD: 'Because Edom has dealt against the house of Judah by taking vengeance, and has greatly offended, and revenged himself on them';
“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
13 therefore thus says the LORD, 'I will stretch out my hand on Edom, and will cut off man and animal from it; and I will make it desolate from Teman; even to Dedan shall they fall by the sword.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
14 I will lay my vengeance on Edom by the hand of my people Israel; and they shall do in Edom according to my anger and according to my wrath; and they shall know my vengeance, says the LORD.'"
Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
15 "Thus says the LORD: 'Because the Philistines have dealt by revenge, and have taken vengeance with despite of soul to destroy with perpetual enmity;
“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
16 therefore thus says the LORD, Look, I will stretch out my hand on the Philistines, and I will cut off the Cherethites, and destroy the remnant of the sea coast.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
17 I will execute great vengeance on them with wrathful rebukes; and they shall know that I am the LORD, when I shall lay my vengeance on them.'"
Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 25 >