< Deuteronomy 8 >

1 You shall observe to do all the commandment which I command you this day, that you may live, and multiply, and go in and possess the land which the LORD swore to your fathers.
Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
2 You shall remember all the way which the LORD your God has led you these forty years in the wilderness, that he might humble you, to prove you, and to know what was in your heart, whether you would keep his commandments, or not.
Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
3 He humbled you, and allowed you to be hungry, and fed you with manna, which you did not know, neither did your fathers know; that he might make you know that humankind cannot live by bread alone, but by every word that proceeds out of the mouth of God shall humankind live.
Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
4 Your clothing did not grow old on you, neither did your foot swell, these forty years.
Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
5 You shall consider in your heart that as a man chastens his son, so the LORD your God chastens you.
Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
6 You shall keep the commandments of the LORD your God, to walk in his ways, and to fear him.
Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
7 For the LORD your God brings you into a good and spacious land, a land of brooks of water, of springs, and underground water flowing into valleys and hills;
Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
8 a land of wheat and barley, and vines and fig trees and pomegranates; a land of olive trees and honey;
dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
9 a land in which you shall eat bread without scarcity, and in which you will lack nothing; a land whose stones are iron, and out of whose hills you may dig copper.
dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
10 You shall eat and be full, and you shall bless the LORD your God for the good land which he has given you.
Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
11 Beware lest you forget the LORD your God, in not keeping his commandments, and his ordinances, and his statutes, which I command you this day:
Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
12 lest, when you have eaten and are full, and have built goodly houses, and lived in them;
kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
13 and when your herds and your flocks multiply, and your silver and your gold is multiplied, and all that you have is multiplied;
ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
14 then your heart be lifted up, and you forget the LORD your God, who brought you forth out of the land of Egypt, out of the house of bondage;
mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
15 who led you through the great and terrible wilderness, with fiery serpents and scorpions, and thirsty ground where there was no water; who brought you forth water out of the rock of flint;
Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
16 who fed you in the wilderness with manna, which your fathers did not know; that he might humble you, and that he might prove you, to do you good at your latter end:
Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
17 and lest you say in your heart, "My power and the might of my hand has gotten me this wealth."
Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
18 But you shall remember the LORD your God, for it is he who gives you power to get wealth; that he may establish his covenant which he swore to your fathers, as at this day.
Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
19 It shall be, if you shall forget the LORD your God, and walk after other gods, and serve them, and worship them, I testify against you this day that you shall surely perish.
Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
20 As the nations that the LORD makes to perish before you, so you shall perish; because you wouldn't listen to the voice of the LORD your God.
Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

< Deuteronomy 8 >