< Deuteronomy 6 >

1 Now this is the commandment, the statutes, and the ordinances, which the LORD your God commanded to teach you, that you might do them in the land where you go over to possess it;
Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
2 that you might fear the LORD your God, to keep all his statutes and his commandments, which I command you, you, and your son, and your son's son, all the days of your life; and that your days may be prolonged.
kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
3 Hear therefore, Israel, and observe to do it; that it may be well with you, and that you may increase mightily, as the LORD, the God of your fathers, has promised to you, in a land flowing with milk and honey.
Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
4 Hear, Israel: the LORD is our God, the LORD is one.
Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
5 And you shall love the LORD your God with all your heart, and with all your soul, and with all your might.
Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
6 These words, which I command you this day, shall be on your heart;
Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
7 and you shall teach them diligently to your children, and shall talk of them when you sit in your house, and when you walk by the way, and when you lie down, and when you rise up.
Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
8 You shall bind them for a sign on your hand, and they shall be for symbols between your eyes.
Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
9 You shall write them on the door posts of your house, and on your gates.
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
10 It shall be, when the LORD your God shall bring you into the land which he swore to your fathers, to Abraham, to Isaac, and to Jacob, to give you, great and goodly cities, which you did not build,
Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
11 and houses full of all good things, which you did not fill, and cisterns dug out, which you did not dig, vineyards and olive trees, which you did not plant, and you shall eat and be full;
nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
12 then beware lest you forget the LORD, who brought you forth out of the land of Egypt, out of the house of bondage.
samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
13 You shall fear the LORD your God; and you shall serve him only, and you shall cling to him, and take oaths by his name.
Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
14 You shall not go after other gods, of the gods of the peoples who are around you;
Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
15 for the LORD your God in the midst of you is a jealous God; lest the anger of the LORD your God be kindled against you, and he destroy you from off the face of the earth.
pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
16 Do not test the LORD your God, as you tested him at Massah.
Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
17 You shall diligently keep the commandments of the LORD your God, and his testimonies, and his statutes, which he has commanded you.
Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
18 You shall do that which is right and good in the sight of the LORD; that it may be well with you, and that you may go in and possess the good land which the LORD swore to your fathers,
Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
19 to thrust out all your enemies from before you, as the LORD has spoken.
kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
20 When your son asks you in time to come, saying, "What do the testimonies, the statutes, and the ordinances, which the LORD our God has commanded you mean?"
Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
21 then you shall tell your son, "We were Pharaoh's bondservants in Egypt: and the LORD brought us out of Egypt with a mighty hand;
Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
22 and the LORD showed great and awesome signs and wonders on Egypt, on Pharaoh, and on all his house, before our eyes;
Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
23 and he brought us out from there, that he might bring us in, to give us the land which he swore to our fathers.
Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
24 The LORD commanded us to do all these statutes, to fear the LORD our God, for our good always, that he might preserve us alive, as at this day.
Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
25 It shall be righteousness to us, if we observe to do all this commandment before the LORD our God, as he has commanded us."
Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”

< Deuteronomy 6 >