< Luke 3 >

1 Now in the fifteenth year of the reign of Tiberius Caesar, when Pontius Pilate was governor of Judea, and Herod was tetrarch of Galilee, his brother Philip, tetrarch of Ituraea and Trachonitis, and Lysanias, tetrarch of Abilene;
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 during the high priesthood of Annas and Caiaphas, the word of God came to John, the son of Zachariah, in the Desert.
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 And Johnwent into all the region about the Jordan, preaching a baptism of repentance for the remission of sins.
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 As it is written in the book of the prophet Isaiah. The voice of one crying in the desert, Prepare the way for God, make straight paths for him.
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 Every ravine shall be filled up, Every hill and mountain shall be laid low, The crooked shall be made straight, And the rough roads smooth;
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 And all flesh shall see the salvation of God.
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 So Johnused to say to the crowd of those who were going out to be baptized by him. "You breed of vipers, who has warned you to flee from the wrath to come?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 Then bring forth fruit befitting your penitence, and do not begin to say to yourselves, "We have Abraham as our father." I tell you that God is able to raise up sons to Abraham out of these stones.
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 And now truly the axe is already laid at the root of the trees. So every tree which is not bearing good fruit is cut down and thrown into the fire."
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 And the crowd began to ask him questions. "What shall we do then?" they asked. In reply he said to them.
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 "If you have two shirts share with him who has none; and let him who has food do the same."
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 There came to him publicans also to be baptized, and they said to him, "Master, what must we do?"
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 And he said to them, "Exact no more than the sum allowed you."
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 The soldiers also repeatedly questioned him, saying, "And we, what shall we do?" "Do not intimidate any one," he replied, "nor lay false charges, and be content with your pay."
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 And while the people were in expectation, and all men were debating in their hearts about John,
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 whether perhaps he were the Christ, Johnanswered, saying to all of them. "I indeed am baptizing you in water, but One is coming after me, mightier than I, whose shoe-latchet I am not worthy to unloose. He shall baptize you in the Holy Ghost and in fire.
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 He has his fan in his hand to cleanse his threshing-floor thoroughly, and to gather the wheat into his storehouse, but the chaff will he burn with unquenchable fire."
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 With many other exhortations then Johndeclared the gospel to the people;
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 but Herod, the Tetrarch, when reproved by him because of Herodias, his brother’s wife, and because of all the wicked deeds that he had done,
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 added yet this above them all that he shut up Johnin prison.
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 Now after all the people had been baptized, and Jesus himself had been baptized and was praying,
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 heaven opened, and the Holy Spirit, in bodily form like a dove, descended upon him. and a voice came out of heaven, saying. "Thou art my Son, dearly beloved; in thee is my delight."
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 And Jesus himself when he began to teach was about thirty years of age. He was the son (as it was supposed) of Joseph, the son of Heli,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 son of Matthat, son of Levi, son of Melchi,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 son of Matthias, son of Nahum, son of Esli,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 son of Mahath, son of Matthias, son of Semein, son of Joseph, son of Joda,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 son of Johann, son of Resa, son of Zerubbabel, son of Shealtiel, son of Neri,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 son of Melchi, son of Addi, son of Cosam, son of Elmadam, son of Er,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 son of Joshua, son of Eliezar, son of Jorim, son of Mathat, son of Levi,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 son of Symeon, son of Judah, son of Joseph, son of Jonan, son of Eliakim,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 son of Melea, son of Menna, son of Mattatha, son of Nathan, son of David,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 son of Jesse, son of Obed, son of Boaz, son of Salmon, son of Nahshon,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 son of Amminadab, son of Admin, son of Arni, son of Hezron, son of Perez, son of Judah,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 son of Jacob, son of Isaac, son of Abraham, son of Terah, son of Nahor,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 son of Serug, son of Reu, son of Peleg, son of Eber, son of Shelah,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 son of Cainan, son of Arpachshad, son of Shem, son of Noah, son of Lamech,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 son of Methuselah, son of Enoch, son of Jared, son of Mahalel, son of Kenan,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 son of Enos, son of Seth, son of Adam, son of God.
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< Luke 3 >