< Psalms 72 >

1 For Solomon. O God, give your judgment to the king, and your righteousness to the king's son;
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 [that he may] judge your people with righteousness, and your poor with judgment.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Let the mountains and the hills raise peace to your people:
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 he shall judge the poor of the people in righteousness, and save the children of the needy; and shall bring low the false accuser.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 And he shall continue as long as the sun, and before the moon for ever.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 He shall come down as rain upon a fleece; and as drops falling upon the earth.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 In his days shall righteousness spring up; and abundance of peace till the moon be removed.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 And he shall have dominion from sea to sea, and from the river to the ends of the earth.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 The Ethiopians shall fall down before him; and his enemies shall lick the dust.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 The kings of Tharsis, and the isles, shall bring presents: the kings of the Arabians and Saba shall offer gifts.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 And all kings shall worship him; all the Gentiles shall serve him.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 For he has delivered the poor from the oppressor; and the needy who had no helper.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 He shall spare the poor and needy, and shall deliver the souls of the needy.
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 He shall redeem their souls from usury and injustice: and their name [shall be] precious before him.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 And he shall live, and there shall be given him of the gold of Arabia: and [men] shall pray for him continually; [and] all the day shall they praise him.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 There shall be an establishment on the earth on the tops of the mountains: the fruit thereof shall be exalted above Libanus, and they of the city shall flourish as grass of the earth.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Let his name be blessed for ever: his name shall endure longer than the sun: and all the tribes of the earth shall be blessed in him: all nations shall call him blessed.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Blessed is the Lord God of Israel, who alone does wonders.
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 And blessed is his glorious name for ever, even for ever and ever: and all the earth shall be filled with his glory. So be it, so be it.
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 The hymns of David the son of Jessae are ended.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Psalms 72 >