< Proverbs 13 >

1 A wise son is obedient to his father: but a disobedient son will be destroyed.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 A good [man] shall eat of the fruits of righteousness: but the lives of transgressors shall perish before their time.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 He that keeps his own mouth keeps his own life: but he that is hasty with his lips shall bring terror upon himself.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Every slothful man desires, but the hands of the active are diligent.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 A righteous man hates an unjust word: but an ungodly man is ashamed, and will have no confidence.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 There are [some] who, having nothing, enrich themselves: and there are [some] who bring themselves down in [the midst of] much wealth.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 A man's own wealth is the ransom of his life: but the poor endures not threatening.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 The righteous always have light: but the light of the ungodly is quenched. Crafty souls go astray in sins: but just men pity, and are merciful.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 A bad man does evil with insolence: but they that are judges of themselves are wise.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Wealth gotten hastily with iniquity is diminished: but he that gathers for himself with godliness shall be increased. The righteous is merciful, and lends.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Better is he that begins to help heartily, than he that promises and leads [another] to hope: for a good desire is a tree of life.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 He that slights a matter shall be slighted of it: but he that fears the commandment has health [of soul]. To a crafty son there shall be nothing good: but a wise servant shall have prosperous doings, and his way shall be directed aright.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 The law of the wise is fountain of life: but the man void of understanding shall die by a snare.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Sound discretion gives favor, and to know the law is the part of a sound understanding: but the ways of scorners tend to destruction.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Every prudent man acts with knowledge: but the fool displays his own mischief.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 A rash king shall fall into mischief: but a wise messenger shall deliver him.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Instruction removes poverty and disgrace: but he that attends to reproofs shall be honored.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 The desires of the godly gladden the soul, but the works of the ungodly are far from knowledge.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 If you walk with wise men you shall be wise: but he that walks with fools shall be known.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Evil shall pursue sinners; but good shall overtake the righteous.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 A good man shall inherit children's children; and the wealth of ungodly men is laid up for the just.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 The righteous shall spend many years in wealth: but the unrighteous shall perish suddenly.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 He that spares the rod hates his son: but he that loves, carefully chastens [him].
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 A just [man] eats and satisfies his soul: but the souls of the ungodly are in lack.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Proverbs 13 >