< Numbers 1 >

1 And the Lord spoke to Moses in the wilderness of Sina, in the tabernacle of witness, on the first day of the second month, in the second year of their departure from the land of Egypt, saying,
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 Take the sum of all the congregation of Israel according to their kindred, according to the houses of their fathers' families, according to their number by their names, according to their heads: every male
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 from twenty years old and upwards, every one that goes forth in the forces of Israel, take account of them with their strength; you and Aaron take account of them.
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 And with you there shall be each one of the rulers according to the tribe of each: they shall be according to the houses of their families.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 And these are the names of the men who shall be present with you; of the tribe of Ruben, Elisur the son of Sediur.
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 Of Symeon, Salamiel the son of Surisadai.
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 Of Juda, Naasson the son of Aminadab.
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 Of Issachar, Nathanael the son of Sogar.
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 Of Zabulon, Eliab the son of Chaelon.
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 Of the sons of Joseph, of Ephraim, Elisama the son of Emiud: of Manasses, Gamaliel the son of Phadasur.
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 Of Benjamin, Abidan the son of Gadeoni.
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 Of Dan, Achiezer the son of Amisadai.
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 Of Aser, Phagaiel the son of Echran.
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 Of Gad, Elisaph the son of Raguel.
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 Of Nephthali, Achire the son of Aenan.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 These were famous men of the congregation, heads of the tribes according to their families: these are heads of thousands in Israel.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 And Moses and Aaron took these men who were called by name.
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 And they assembled all the congregation on the first day of the month in the second year; and they registered them after their lineage, after their families, after the number of their names, from twenty years old and upwards, every male according to their number:
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 as the Lord commanded Moses, so they were numbered in the wilderness of Sina.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 And the sons of Ruben the firstborn of Israel according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their heads, were—all males from twenty years old and upward, every one that went out with the host—
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 the numbering of them of the tribe of Ruben, was forty-six thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 For the children of Symeon according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes out with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 the numbering of them of the tribe of Symeon, was fifty-nine thousand and three hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 For the sons of Juda according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 the numbering of them of the tribe of Juda, was seventy-four thousand and six hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 For the sons of Issachar according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 the numbering of them of the tribe of Issachar, was fifty-four thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 For the sons of Zabulon according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes out with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 the numbering of them of the tribe of Zabulon, was fifty-seven thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 For the sons of Joseph, the sons of Ephraim, according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes out with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 the numbering of them of the tribe of Ephraim, was forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 For the sons of Manasse according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes out with the host,
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 the numbering of them of the tribe of Manasse, was thirty-two thousand and two hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 For the sons of Benjamin according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, every male from twenty years old and upward, every one that goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 the numbering of them of the tribe of Benjamin, was thirty-five thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 For the sons of Gad according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 the numbering of them of the tribe of Gad, was forty and five thousand and six hundred and fifty.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 For the sons of Dan according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, all males from twenty years old and upward, every one that goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 the numbering of them of the tribe of Dan, was sixty and two thousand and seven hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 For the sons of Aser according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, every male from twenty years old and upward, every one that goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 the numbering of them of the tribe of Aser, was forty and one thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 For the sons of Nephthali according to their kindred, according to their divisions, according to the houses of their families, according to the number of their names, according to their polls, every male from twenty years old and upward, every one who goes forth with the host,
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 the numbering of them of the tribe of Nephthali, was fifty-three thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 This is the numbering which Moses and Aaron and the rulers of Israel, being twelve men, conducted: there was a man for each tribe, they were according to the tribe of the houses of their family.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 And the whole numbering of the children of Israel with their host from twenty years old and upward, every one that goes out to set himself in battle array in Israel, came to
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 six hundred thousand and three thousand and five hundred and fifty.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 But the Levites of the tribe of their family were not counted among the children of Israel.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 And the Lord spoke to Moses, saying,
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 See, you shall not muster the tribe of Levi, and you shall not take their numbers, in the midst of the children of Israel.
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 And do you set the Levites over the tabernacle of witness, and over all its furniture, and over all things that are in it; and they shall do service in it, and they shall encamp round about the tabernacle.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 And in removing the tabernacle, the Levites shall take it down, and in pitching the tabernacle they shall set it up: and let the stranger that advances [to touch it] die.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 And the children of Israel shall encamp, every man in his own order, and every man according to his company, with their host.
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 But let the Levites encamp round about the tabernacle of witness fronting it, and [so] there shall be no sin among the children of Israel; and the Levites themselves shall keep the guard of the tabernacle of witness.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 And the children of Israel did according to all that the Lord commanded Moses and Aaron, so did they.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

< Numbers 1 >