< Job 10 >

1 Weary in my soul, I will pour my words with groans upon him: I will speak being straitened in the bitterness of my soul.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 And I will say to the Lord, Do not teach me to be impious; and therefore have you thus judged me?
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Is it good before you if I be unrighteous? for you have disowned the work of your hands, and attended to the counsel of the ungodly.
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Or do you see as a mortal sees? or will you look as a man sees?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Or is your life human, or your years [the years] of a man,
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 that you have enquired into mine iniquity, and searched out my sins?
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 For you know that I have not committed iniquity: but who is he that can deliver out of your hands?
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Your hands have formed me and made me; afterwards you did change [your mind], and strike me.
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Remember that you have made me [as] clay, and you do turn me again to earth.
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Hast you not poured me out like milk, and curdled me like cheese?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 And you did clothe me with skin and flesh, and frame me with bones and sinews.
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 And you did bestow upon me life and mercy, and your oversight has preserved my spirit.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Having these things in yourself, I know that you can do all things; for nothing is impossible with you.
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 And if I should sin, you watch me; and you have not cleared me from iniquity.
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 Or if I should be ungodly, woe is me: and if I should be righteous, I can’t lift myself up, for I am full of dishonor.
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 For I am hunted like a lion for slaughter; for again you have changed and are terribly destroying me;
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 renewing against me my torture: and you have dealt with me in great anger, and you have brought trials upon me.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Why then did you bring me out of the womb? and why did I not die, and no eye see me,
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 and I become as if I had not been? for why was I not carried from the womb to the grave?
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Is not the time of my life short? suffer me to rest a little,
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 before I go whence I shall not return, to a land of darkness and gloominess;
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 to a land of perpetual darkness, where there is no light, neither [can any one] see the life of mortals.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Job 10 >