< Ecclesiastes 4 >

1 So I returned, and saw all the oppressions that were done under the sun: and behold the tear of the oppressed, and they had no comforter; and on the side of them that oppressed them was power; but they had no comforter:
Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano: ndinaona misozi ya anthu opsinjika, ndipo iwo alibe owatonthoza; mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo ndipo iwonso analibe owatonthoza.
2 and I praised all the dead that had already died more than the living, as many as are alive until now.
Ndipo ndinanena kuti akufa, amene anafa kale, ndi osangalala kuposa amoyo, amene akanalibe ndi moyo.
3 Better also than both these is he who has not yet been, who has not seen all the evil work that is done under the sun.
Koma wopambana onsewa ndi amene sanabadwe, amene sanaone zoyipa zimene chimachitika pansi pano.
4 And I saw all labor, and all the diligent work, that this is a man's envy from his neighbor. This is also vanity and waywardness of spirit.
Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 The fool folds his hands together, and eats his own flesh.
Chitsiru chimangoti manja ake lobodo ndi kudzipha chokha ndi njala.
6 Better is a handful of rest than two handfuls of trouble and waywardness of spirit.
Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere, kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto, ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.
7 So I returned, and saw vanity under the sun.
Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 There is one [alone], and there is not a second; yes, he has neither son nor brother: yet there is no end to all his labor; neither is his eye satisfied with wealth; and for whom do I labor, and deprive my soul of good? this is also vanity, and an evil trouble.
Panali munthu amene anali yekhayekha; analibe mwana kapena mʼbale. Ntchito yake yolemetsa sinkatha, ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake. Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?” Izinso ndi zopandapake, zosasangalatsa!
9 Two [are] better than one, [seeing] they have a good reward for their labor.
Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha, chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:
10 For if they fall, the one will lift up his fellow: but woe to him that is alone when he falls, and there is not a second to lift him up.
Ngati winayo agwa, mnzakeyo adzamudzutsa. Koma tsoka kwa munthu amene agwa ndipo alibe wina woti amudzutse!
11 Also if two should lie together, they also get heat: but how shall one be warmed [alone?]
Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana. Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?
12 And if one should prevail against [him], the two shall withstand him; and a threefold cord shall not be quickly broken.
Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa, koma anthu awiri akhoza kudziteteza. Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.
13 Better is a poor and wise child than an old and foolish king, who knows not how to take heed any longer.
Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo.
14 For he shall come forth out of the house of the prisoners to reign, because [he] also that was in his kingdom has become poor.
Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo.
15 I saw all the living who were walking under the sun, with the second youth who shall stand up in each one's place.
Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu.
16 There is no end to all the people, to all who were before them: and the last shall not rejoice in him: for this also is vanity and waywardness of spirit.
Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.

< Ecclesiastes 4 >