< Proverbs 24 >

1 Be not you envious against evil men, neither desire to be with them.
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 For their heart studies destruction, and their lips talk of mischief.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Through wisdom is an house built; and by understanding it is established:
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 And by knowledge shall the chambers be filled with all precious and pleasant riches.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 A wise man is strong; yes, a man of knowledge increases strength.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 For by wise counsel you shall make your war: and in multitude of counsellors there is safety.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Wisdom is too high for a fool: he opens not his mouth in the gate.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 He that devises to do evil shall be called a mischievous person.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 The thought of foolishness is sin: and the scorner is an abomination to men.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 If you faint in the day of adversity, your strength is small.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 If you forbear to deliver them that are drawn to death, and those that are ready to be slain;
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 If you say, Behold, we knew it not; does not he that ponders the heart consider it? and he that keeps your soul, does not he know it? and shall not he render to every man according to his works?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 My son, eat you honey, because it is good; and the honeycomb, which is sweet to your taste:
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 So shall the knowledge of wisdom be to your soul: when you have found it, then there shall be a reward, and your expectation shall not be cut off.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Lay not wait, O wicked man, against the dwelling of the righteous; spoil not his resting place:
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 For a just man falls seven times, and rises up again: but the wicked shall fall into mischief.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Rejoice not when your enemy falls, and let not your heart be glad when he stumbles:
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Lest the LORD see it, and it displease him, and he turn away his wrath from him.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Fret not yourself because of evil men, neither be you envious at the wicked:
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 For there shall be no reward to the evil man; the candle of the wicked shall be put out.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 My son, fear you the LORD and the king: and meddle not with them that are given to change:
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 For their calamity shall rise suddenly; and who knows the ruin of them both?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 These things also belong to the wise. It is not good to have respect of persons in judgment.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 He that says to the wicked, You are righteous; him shall the people curse, nations shall abhor him:
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 But to them that rebuke him shall be delight, and a good blessing shall come on them.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Every man shall kiss his lips that gives a right answer.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Prepare your work without, and make it fit for yourself in the field; and afterwards build your house.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Be not a witness against your neighbor without cause; and deceive not with your lips.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Say not, I will do so to him as he has done to me: I will render to the man according to his work.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 I went by the field of the slothful, and by the vineyard of the man void of understanding;
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 And, see, it was all grown over with thorns, and nettles had covered the face thereof, and the stone wall thereof was broken down.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Then I saw, and considered it well: I looked on it, and received instruction.
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 Yet a little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to sleep:
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 So shall your poverty come as one that travels; and your want as an armed man.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Proverbs 24 >