< Psalms 99 >

1 The LORD reigneth; let the peoples tremble; He is enthroned upon the cherubim; let the earth quake.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 The LORD is great in Zion; and He is high above all the peoples.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Let them praise Thy name as great and awful; Holy is He.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 The strength also of the king who loveth justice — Thou hast established equity, Thou hast executed justice and righteousness in Jacob.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Exalt ye the LORD our God, and prostrate yourselves at His footstool; Holy is He.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moses and Aaron among His priests, and Samuel among them that call upon His name, did call upon the LORD, and He answered them.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 He spoke unto them in the pillar of cloud; they kept His testimonies, and the statute that He gave them.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 O LORD our God, Thou didst answer them; a forgiving God wast Thou unto them, though Thou tookest vengeance of their misdeeds.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Exalt ye the LORD our God, and worship at His holy hill; for the LORD our God is holy.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

< Psalms 99 >