< Psalms 75 >

1 For the Leader; Al-tashheth. A Psalm of Asaph, a Song. We give thanks unto Thee, O God, we give thanks, and Thy name is near; men tell of Thy wondrous works.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 'When I take the appointed time, I Myself will judge with equity.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 When the earth and all the inhabitants thereof are dissolved, I Myself establish the pillars of it.' (Selah)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 I say unto the arrogant: 'Deal not arrogantly'; and to the wicked: 'Lift not up the horn.'
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Lift not up your horn on high; speak not insolence with a haughty neck.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 For neither from the east, nor from the west, nor yet from the wilderness, cometh lifting up.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 For God is judge; He putteth down one, and lifteth up another.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 For in the hand of the LORD there is a cup, with foaming wine, full of mixture, and He poureth out of the same; surely the dregs thereof, all the wicked of the earth shall drain them, and drink them.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 But as for me, I will declare for ever, I will sing praises to the God of Jacob.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 All the horns of the wicked also will I cut off; but the horns of the righteous shall be lifted up.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psalms 75 >