< Psalms 129 >

1 A Song of Ascents. 'Much have they afflicted me from my youth up', let Israel now say;
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 'Much have they afflicted me from my youth up; but they have not prevailed against me.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 The plowers plowed upon my back; they made long their furrows.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 The LORD is righteous; He hath cut asunder the cords of the wicked.'
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 Let them be ashamed and turned backward, all they that hate Zion.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Let them be as the grass upon the housetops, which withereth afore it springeth up;
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 Wherewith the reaper filleth not his hand, nor he that bindeth sheaves his bosom.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 Neither do they that go by say: 'The blessing of the LORD be upon you; we bless you in the name of the LORD.'
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< Psalms 129 >