< Numbers 31 >

1 And the LORD spoke unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 'Avenge the children of Israel of the Midianites; afterward shalt thou be gathered unto thy people.'
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 And Moses spoke unto the people, saying: 'Arm ye men from among you for the war, that they may go against Midian, to execute the LORD'S vengeance on Midian.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Of every tribe a thousand, throughout all the tribes of Israel, shall ye send to the war.'
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 So there were delivered, out of the thousands of Israel, a thousand of every tribe, twelve thousand armed for war.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 And Moses sent them, a thousand of every tribe, to the war, them and Phinehas the son of Eleazar the priest, to the war, with the holy vessels and the trumpets for the alarm in his hand.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 And they warred against Midian, as the LORD commanded Moses; and they slew every male.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 And they slew the kings of Midian with the rest of their slain: Evi, and Rekem, and Zur, and Hur, and Reba, the five kings of Midian; Balaam also the son of Beor they slew with the sword.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 And the children of Israel took captive the women of Midian and their little ones; and all their cattle, and all their flocks, and all their goods, they took for a prey.
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 And all their cities in the places wherein they dwelt, and all their encampments, they burnt with fire.
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 And they took all the spoil, and all the prey, both of man and of beast.
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 And they brought the captives, and the prey, and the spoil, unto Moses, and unto Eleazar the priest, and unto the congregation of the children of Israel, unto the camp, unto the plains of Moab, which are by the Jordan at Jericho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 And Moses, and Eleazar the priest, and all the princes of the congregation, went forth to meet them without the camp.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 And Moses was wroth with the officers of the host, the captains of thousands and the captains of hundreds, who came from the service of the war.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 And Moses said unto them: 'Have ye saved all the women alive?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Behold, these caused the children of Israel, through the counsel of Balaam, to revolt so as to break faith with the LORD in the matter of Peor, and so the plague was among the congregation of the LORD.
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Now therefore kill every male among the little ones, and kill every woman that hath known man by lying with him.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 But all the women children, that have not known man by lying with him, keep alive for yourselves.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 And encamp ye without the camp seven days; whosoever hath killed any person, and whosoever hath touched any slain, purify yourselves on the third day and on the seventh day, ye and your captives.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 And as to every garment, and all that is made of skin, and all work of goats' hair, and all things made of wood, ye shall purify.'
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 And Eleazar the priest said unto the men of war that went to the battle: 'This is the statute of the law which the LORD hath commanded Moses:
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 Howbeit the gold, and the silver, the brass, the iron, the tin, and the lead,
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 every thing that may abide the fire, ye shall make to go through the fire, and it shall be clean; nevertheless it shall be purified with the water of sprinkling; and all that abideth not the fire ye shall make to go through the water.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 And ye shall wash your clothes on the seventh day, and ye shall be clean, and afterward ye may come into the camp.'
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 And the LORD spoke unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 'Take the sum of the prey that was taken, both of man and of beast, thou, and Eleazar the priest, and the heads of the fathers' houses of the congregation;
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 and divide the prey into two parts: between the men skilled in war, that went out to battle, and all the congregation;
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 and levy a tribute unto the LORD of the men of war that went out to battle: one soul of five hundred, both of the persons, and of the beeves, and of the asses, and of the flocks;
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 take it of their half, and give it unto Eleazar the priest, as a portion set apart for the LORD.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 And of the children of Israel's half, thou shalt take one drawn out of every fifty, of the persons, of the beeves, of the asses, and of the flocks, even of all the cattle, and give them unto the Levites, that keep the charge of the tabernacle of the LORD.'
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 And Moses and Eleazar the priest did as the LORD commanded Moses.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 Now the prey, over and above the booty which the men of war took, was six hundred thousand and seventy thousand and five thousand sheep,
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 and threescore and twelve thousand beeves,
Ngʼombe 72,000,
34 and threescore and one thousand asses,
abulu 61,000,
35 and thirty and two thousand persons in all, of the women that had not known man by lying with him.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 And the half, which was the portion of them that went out to war, was in number three hundred thousand and thirty thousand and seven thousand and five hundred sheep.
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 And the LORD'S tribute of the sheep was six hundred and threescore and fifteen.
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 And the beeves were thirty and six thousand, of which the LORD'S tribute was threescore and twelve.
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 And the asses were thirty thousand and five hundred, of which the LORD'S tribute was threescore and one.
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 And the persons were sixteen thousand, of whom the LORD'S tribute was thirty and two persons.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 And Moses gave the tribute, which was set apart for the LORD, unto Eleazar the priest, as the LORD commanded Moses.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 And of the children of Israel's half, which Moses divided off from the men that warred —
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 now the congregation's half was three hundred thousand and thirty thousand and seven thousand and five hundred sheep,
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 and thirty and six thousand beeves,
ngʼombe 36,000,
45 and thirty thousand and five hundred asses,
abulu 30,500,
46 and sixteen thousand persons —
anthu 16,000.
47 even of the children of Israel's half, Moses took one drawn out of every fifty, both of man and of beast, and gave them unto the Levites, that kept the charge of the tabernacle of the LORD; as the LORD commanded Moses.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 And the officers that were over the thousands of the host, the captains of thousands, and the captains of hundreds, came near unto Moses;
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 and they said unto Moses: 'Thy servants have taken the sum of the men of war that are under our charge, and there lacketh not one man of us.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 And we have brought the LORD'S offering, what every man hath gotten, of jewels of gold, armlets, and bracelets, signet-rings, ear-rings, and girdles, to make atonement for our souls before the LORD.'
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 And Moses and Eleazar the priest took the gold of them, even all wrought jewels.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 And all the gold of the gift that they set apart for the LORD, of the captains of thousands, and of the captains of hundreds, was sixteen thousand seven hundred and fifty shekels. —
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 For the men of war had taken booty, every man for himself. —
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 And Moses and Eleazar the priest took the gold of the captains of thousands and of hundreds, and brought it into the tent of meeting, for a memorial for the children of Israel before the LORD.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

< Numbers 31 >