< Leviticus 10 >

1 And Nadab and Abihu, the sons of Aaron, took each of them his censer, and put fire therein, and laid incense thereon, and offered strange fire before the LORD, which He had not commanded them.
Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
2 And there came forth fire from before the LORD, and devoured them, and they died before the LORD.
Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
3 Then Moses said unto Aaron: 'This is it that the LORD spoke, saying: Through them that are nigh unto Me I will be sanctified, and before all the people I will be glorified.' And Aaron held his peace.
Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
4 And Moses called Mishael and Elzaphan, the sons of Uzziel the uncle of Aaron, and said unto them: 'Draw near, carry your brethren from before the sanctuary out of the camp.'
Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
5 So they drew near, and carried them in their tunics out of the camp, as Moses had said.
Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
6 And Moses said unto Aaron, and unto Eleazar and unto Ithamar, his sons: 'Let not the hair of your heads go loose, neither tend your clothes, that ye die not, and that He be not wroth with all the congregation; but let your brethren, the whole house of Israel, bewail the burning which the LORD hath kindled.
Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
7 And ye shall not go out from the door of the tent of meeting, lest ye die; for the anointing oil of the LORD is upon you.' And they did according to the word of Moses.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
8 And the LORD spoke unto Aaron, saying:
Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
9 'Drink no wine nor strong drink, thou, nor thy sons with thee, when ye go into the tent of meeting, that ye die not; it shall be a statute forever throughout your generations.
“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
10 And that ye may put difference between the holy and the common, and between the unclean and the clean;
Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
11 and that ye may teach the children of Israel all the statutes which the LORD hath spoken unto them by the hand of Moses.'
ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
12 And Moses spoke unto Aaron, and unto Eleazar and unto Ithamar, his sons that were left: 'Take the meal-offering that remaineth of the offerings of the LORD made by fire, and eat it without leaven beside the altar; for it is most holy.
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
13 And ye shall eat it in a holy place, because it is thy due, and thy sons' due, of the offerings of the LORD made by fire; for so I am commanded.
Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
14 And the breast of waving and the thigh of heaving shall ye eat in a clean place; thou, and thy sons, and thy daughters with thee; for they are given as thy due, and thy sons' due, out of the sacrifices of the peace-offerings of the children of Israel.
Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
15 The thigh of heaving and the breast of waving shall they bring with the offerings of the fat made by fire, to wave it for a wave-offering before the LORD; and it shall be thine, and thy sons' with thee, as a due for ever; as the LORD hath commanded.'
Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
16 And Moses diligently inquired for the goat of the sin-offering, and, behold, it was burnt; and he was angry with Eleazar and with Ithamar, the sons of Aaron that were left, saying:
Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
17 'Wherefore have ye not eaten the sin-offering in the place of the sanctuary, seeing it is most holy, and He hath given it you to bear the iniquity of the congregation, to make atonement for them before the LORD?
“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
18 Behold, the blood of it was not brought into the sanctuary within; ye should certainly have eaten it in the sanctuary, as I commanded.'
Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
19 And Aaron spoke unto Moses: 'Behold, this day have they offered their sin-offering and their burnt-offering before the LORD, and there have befallen me such things as these; and if I had eaten the sin-offering to-day, would it have been well-pleasing in the sight of the LORD?
Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
20 And when Moses heard that, it was well-pleasing in his sight.
Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

< Leviticus 10 >