< Jeremiah 32 >

1 The word that came to Jeremiah from the LORD in the tenth year of Zedekiah king of Judah, which was the eighteenth year of Nebuchadrezzar.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 Now at that time the king of Babylon's army was besieging Jerusalem; and Jeremiah the prophet was shut up in the court of the guard, which was in the king of Judah's house.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 For Zedekiah king of Judah had shut him up, saying: 'Wherefore dost thou prophesy, and say: Thus saith the LORD: Behold, I will give this city into the hand of the king of Babylon, and he shall take it;
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 and Zedekiah king of Judah shall not escape out of the hand of the Chaldeans, but shall surely be delivered into the hand of the king of Babylon, and shall speak with him mouth to mouth, and his eyes shall behold his eyes;
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 and he shall lead Zedekiah to Babylon, and there shall he be until I remember him, saith the LORD; though ye fight with the Chaldeans, ye shall not prosper?'
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 And Jeremiah said: 'The word of the LORD came unto me, saying:
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 Behold, Hanamel, the son of Shallum thine uncle, shall come unto thee, saying: Buy thee my field that is in Anathoth; for the right of redemption is thine to buy it.'
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 So Hanamel mine uncle's son came to me in the court of the guard according to the word of the LORD, and said unto me: 'Buy my field, I pray thee, that is in Anathoth, which is in the land of Benjamin; for the right of inheritance is thine, and the redemption is thine; buy it for thyself.' Then I knew that this was the word of the LORD.
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 And I bought the field that was in Anathoth of Hanamel mine uncle's son, and weighed him the money, even seventeen shekels of silver.
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 And I subscribed the deed, and sealed it, and called witnesses, and weighed him the money in the balances.
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 So I took the deed of the purchase, both that which was sealed, containing the terms and conditions, and that which was open;
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 and I delivered the deed of the purchase unto Baruch the son of Neriah, the son of Mahseiah, in the presence of Hanamel mine uncle 's son, and in the presence of the witnesses that subscribed the deed of the purchase, before all the Jews that sat in the court of the guard.
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 And I charged Baruch before them, saying:
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 'Thus saith the LORD of hosts, the God of Israel: Take these deeds, this deed of the purchase, both that which is sealed, and this deed which is open, and put them in an earthen vessel; that they may continue many days.
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 For thus saith the LORD of hosts, the God of Israel: Houses and fields and vineyards shall yet again be bought in this land.'
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 Now after I had delivered the deed of the purchase unto Baruch the son of Neriah, I prayed unto the LORD, saying:
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 'Ah Lord GOD! behold, Thou hast made the heaven and the earth by Thy great power and by Thy outstretched arm; there is nothing too hard for Thee;
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 who showest mercy unto thousands, and recompensest the iniquity of the fathers into the bosom of their children after them; the great, the mighty God, the LORD of hosts is His name;
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 great in counsel, and mighty in work; whose eyes are open upon all the ways of the sons of men, to give every one according to his ways, and according to the fruit of his doings;
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 who didst set signs and wonders in the land of Egypt, even unto this day, and in Israel and among other men; and madest Thee a name, as at this day;
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 and didst bring forth Thy people Israel out of the land of Egypt with signs, and with wonders, and with a strong hand, and with an outstretched arm, and with great terror;
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 and gavest them this land, which Thou didst swear to their fathers to give them, a land flowing with milk and honey;
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 and they came in, and possessed it; but they hearkened not to Thy voice, neither walked in Thy law; they have done nothing of all that Thou commandedst them to do; therefore Thou hast caused all this evil to befall them;
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 behold the mounds, they are come unto the city to take it; and the city is given into the hand of the Chaldeans that fight against it, because of the sword, and of the famine, and of the pestilence; and what Thou hast spoken is come to pass; and, behold, Thou seest it.
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 Yet Thou hast said unto me, O Lord GOD: Buy thee the field for money, and call witnesses; whereas the city is given into the hand of the Chaldeans.'
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 Then came the word of the LORD unto Jeremiah, saying:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 'Behold, I am the LORD, the God of all flesh; is there any thing too hard for Me?
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Therefore thus saith the LORD: Behold, I will give this city into the hand of the Chaldeans, and into the hand of Nebuchadrezzar king of Babylon, and he shall take it;
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 and the Chaldeans, that fight against this city, shall come and set this city on fire, and burn it, with the houses, upon whose roofs they have offered unto Baal, and poured out drink-offerings unto other gods, to provoke Me.
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 For the children of Israel and the children of Judah have only done that which was evil in My sight from their youth; for the children of Israel have only provoked Me with the work of their hands, saith the LORD.
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 For this city hath been to Me a provocation of Mine anger and of My fury from the day that they built it even unto this day, that I should remove it from before My face;
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 because of all the evil of the children of Israel and of the children of Judah, which they have done to provoke Me, they, their kings, their princes, their priests, and their prophets, and the men of Judah, and the inhabitants of Jerusalem.
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 And they have turned unto Me the back, and not the face; and though I taught them, teaching them betimes and often, yet they have not hearkened to receive instruction.
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 But they set their abominations in the house whereupon My name is called, to defile it.
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 And they built the high places of Baal, which are in the valley of the son of Hinnom, to set apart their sons and their daughters unto Molech; which I commanded them not, neither came it into My mind, that they should do this abomination; to cause Judah to sin.
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 And now therefore thus saith the LORD, the God of Israel, concerning this city, whereof ye say: It is given into the hand of the king of Babylon by the sword, and by the famine, and by the pestilence:
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Behold, I will gather them out of all the countries, whither I have driven them in Mine anger, and in My fury, and in great wrath; and I will bring them back unto this place, and I will cause them to dwell safely;
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 and they shall be My people, and I will be their God;
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 and I will give them one heart and one way, that they may fear Me for ever; for the good of them, and of their children after them;
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 and I will make an everlasting covenant with them, that I will not turn away from them, to do them good; and I will put My fear in their hearts, that they shall not depart from Me.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 Yea, I will rejoice over them to do them good, and I will plant them in this land in truth with My whole heart and with My whole soul.
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 For thus saith the LORD: Like as I have brought all this great evil upon this people, so will I bring upon them all the good that I have promised them.
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 And fields shall be bought in this land, whereof ye say: It is desolate, without man or beast; it is given into the hand of the Chaldeans.
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 Men shall buy fields for money, and subscribe the deeds, and seal them, and call witnesses, in the land of Benjamin, and in the places about Jerusalem, and in the cities of Judah, and in the cities of the hill-country, and in the cities of the Lowland, and in the cities of the South; for I will cause their captivity to return, saith the LORD.'
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< Jeremiah 32 >