< Isaiah 12 >

1 And in that day thou shalt say: 'I will give thanks unto Thee, O LORD; for though Thou was angry with me, Thine anger is turned away, and Thou comfortest me.
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
2 Behold, God is my salvation; I will trust, and will not be afraid; for GOD the LORD is my strength and song; and He is become my salvation.'
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 Therefore with joy shall ye draw water out of the wells of salvation.
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 And in that day shall ye say: 'Give thanks unto the LORD, proclaim His name, declare His doings among the peoples, make mention that His name is exalted.
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Sing unto the LORD; for He hath done gloriously; this is made known in all the earth.
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Cry aloud and shout, thou inhabitant of Zion, for great is the Holy One of Israel in the midst of thee.'
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

< Isaiah 12 >