< Ezekiel 38 >

1 And the word of the LORD came unto me, saying:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 'Son of man, set thy face toward Gog, of the land of Magog, the chief prince of Meshech and Tubal, and prophesy against him,
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 and say: Thus saith the Lord GOD: Behold, I am against thee, O Gog, chief prince of Meshech and Tubal;
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 and I will turn thee about, and put hooks into thy jaws, and I will bring thee forth, and all thine army, horses and horsemen, all of them clothed most gorgeously, a great company with buckler and shield, all of them handling swords:
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Persia, Cush, and Put with them, all of them with shield and helmet;
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer, and all his bands; the house of Togarmah in the uttermost parts of the north, and all his bands; even many peoples with thee.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Be thou prepared, and prepare for thyself, thou, and all thy company that are assembled unto thee, and be thou guarded of them.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 After many days thou shalt be mustered for service, in the latter years thou shalt come against the land that is brought back from the sword, that is gathered out of many peoples, against the mountains of Israel, which have been a continual waste; but it is brought forth out of the peoples, and they dwell safely all of them.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 And thou shalt ascend, thou shalt come like a storm, thou shalt be like a cloud to cover the land, thou, and all thy bands, and many peoples with thee.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Thus saith the Lord GOD: It shall come to pass in that day, that things shall come into thy mind, and thou shalt devise an evil device;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 and thou shalt say: I will go up against the land of unwalled villages; I will come upon them that are at quiet, that dwell safely, all of them dwelling without walls, and having neither bars nor gates;
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 to take the spoil and to take the prey; to turn thy hand against the waste places that are now inhabited, and against the people that are gathered out of the nations, that have gotten cattle and goods, that dwell in the middle of the earth.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Sheba, and Dedan, and the merchants of Tarshish, with all the magnates thereof, shall say unto thee: Comest thou to take the spoil? hast thou assembled thy company to take the prey? to carry away silver and gold, to take away cattle and goods, to take great spoil?
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Therefore, son of man, prophesy, and say unto Gog: Thus saith the Lord GOD: In that day when My people Israel dwelleth safely, shalt thou not know it?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 And thou shalt come from thy place out of the uttermost parts of the north, thou, and many peoples with thee, all of them riding upon horses, a great company and a mighty army;
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 and thou shalt come up against My people Israel, as a cloud to cover the land; it shall be in the end of days, and I will bring thee against My land, that the nations may know Me, when I shall be sanctified through thee, O Gog, before their eyes.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Thus saith the Lord GOD: Art thou he of whom I spoke in old time by My servants the prophets of Israel, that prophesied in those days for many years, that I would bring thee against them?
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 And it shall come to pass in that day, when Gog shall come against the land of Israel, saith the Lord GOD, that My fury shall arise up in My nostrils.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 For in My jealousy and in the fire of My wrath have I spoken: Surely in that day there shall be a great shaking in the land of Israel;
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 so that the fishes of the sea, and the fowls of the heaven, and the beasts of the field and all creeping things that creep upon the ground, and all the men that are upon the face of the earth, shall shake at My presence, and the mountains shall be thrown down, and the steep places shall fall, and every wall shall fall to the ground.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 And I will call for a sword against him throughout all my mountains, saith the Lord GOD; every man's sword shall be against his brother.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 And I will plead against him with pestilence and with blood; and I will cause to rain upon him, and upon his bands, and upon the many peoples that are with him, an overflowing shower, and great hailstones, fire, and brimstone.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Thus will I magnify Myself, and sanctify Myself, and I will make Myself known in the eyes of many nations; and they shall know that I am the LORD.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 38 >