< Deuteronomy 19 >

1 When the LORD thy God shall cut off the nations, whose land the LORD thy God giveth thee, and thou dost succeed them, and dwell in their cities, and in their houses;
Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
2 thou shalt separate three cities for thee in the midst of thy land, which the LORD thy GOD giveth thee to possess it.
mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
3 Thou shalt prepare thee the way, and divide the borders of thy land, which the LORD thy God causeth thee to inherit, into three parts, that every manslayer may flee thither.
Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
4 And this is the case of the manslayer, that shall flee thither and live: whoso killeth his neighbour unawares, and hated him not in time past;
Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
5 as when a man goeth into the forest with his neighbour to hew wood, and his hand fetcheth a stroke with the axe to cut down the tree, and the head slippeth from the helve, and lighteth upon his neighbour, that he die; he shall flee unto one of these cities and live;
Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
6 lest the avenger of blood pursue the manslayer, while his heart is hot, and overtake him, because the way is long, and smite him mortally; whereas he was not deserving of death, inasmuch as he hated him not in time past.
Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
7 Wherefore I command thee, saying: 'Thou shalt separate three cities for thee.'
Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
8 And if the LORD thy God enlarge thy border, as He hath sworn unto thy fathers, and give thee all the land which He promised to give unto thy fathers —
Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
9 if thou shalt keep all this commandment to do it, which I command thee this day, to love the LORD thy God, and to walk ever in His ways — then shalt thou add three cities more for thee, beside these three;
chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
10 that innocent blood be not shed in the midst of thy land, which the LORD thy God giveth thee for an inheritance, and so blood be upon thee.
Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
11 But if any man hate his neighbour, and lie in wait for him, and rise up against him, and smite him mortally that he die; and he flee into one of these cities;
Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
12 then the elders of his city shall send and fetch him thence, and deliver him into the hand of the avenger of blood, that he may die.
akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
13 Thine eye shall not pity him, but thou shalt put away the blood of the innocent from Israel, that it may go well with thee.
Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
14 Thou shalt not remove thy neighbour's landmark, which they of old time have set, in thine inheritance which thou shalt inherit, in the land that the LORD thy God giveth thee to possess it.
Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
15 One witness shall not rise up against a man for any iniquity, or for any sin, in any sin that he sinneth; at the mouth of two witnesses, or at the mouth of three witnesses, shall a matter be establishment
Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
16 If an unrighteous witness rise up against any man to bear perverted witness against him;
Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
17 then both the men, between whom the controversy is, shall stand before the LORD, before the priests and the judges that shall be in those days.
anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
18 And the judges shall inquire diligently; and, behold, if the witness be a false witness, and hath testified falsely against his brother;
Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
19 then shall ye do unto him, as he had purposed to do unto his brother; so shalt thou put away the evil from the midst of thee.
ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
20 And those that remain shall hear, and fear, and shall henceforth commit no more any such evil in the midst of thee.
Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
21 And thine eye shall not pity: life for life, eye for eye, tooth for tooth, hand for hand, foot for foot.
Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.

< Deuteronomy 19 >