< 2 Samuel 15 >

1 And it came to pass after this, that Absalom prepared him a chariot and horses, and fifty men to run before him.
Patapita nthawi, Abisalomu anadzipezera galeta ndi akavalo pamodzi ndi amuna makumi asanu amene amathamanga patsogolo pake.
2 And Absalom used to rise up early, and stand beside the way of the gate; and it was so, that when any man had a suit which should come to the king for judgment, then Absalom called unto him, and said: 'Of what city art thou?' And he said: 'Thy servant is of one of the tribes of Israel.'
Iye amadzuka mmamawa ndi kuyima pa njira yopita ku chipata cha mzinda. Munthu wina aliyense akakhala ndi zodandaula zopita nazo kwa mfumu kuti akaweruze, Abisalomu amamuyitana iye ndi kumufunsa kuti, “Kodi ukuchokera ku limodzi mwa mafuko a Israeli?”
3 And Absalom said unto him: 'See, thy matters are good and right; but there is no man deputed of the king to hear thee.'
Kenaka Abisalomu amanena kwa iye kuti, “Taona, madandawulo ako ndi abwino ndi oyenera, koma palibe woyimira mfumu woti akumvere.”
4 Absalom said moreover: 'Oh that I were made judge in the land, that every man who hath any suit or cause might come unto me, and I would do him justice!'
Ndipo Abisalomu amawonjezera kunena kuti, “Ine ndikanangosankhidwa kukhala woweruza mʼdziko muno bwenzi munthu aliyense amene ali ndi madandawulo kapena milandu akubwera kwa ine ndipo ndikanaonetsetsa kuti chilungamo chachitika.”
5 And it was so, that when any man came nigh to prostrate himself before him, he put forth his hand, and took hold of him, and kissed him.
Ndipo nthawi zonse amati munthu akasendera pafupi ndi kumugwandira, Abisalomu amatambalitsa dzanja lake, kumuyimiritsa munthuyo ndi kupsompsona.
6 And on this manner did Absalom to all Israel that came to the king for judgment; so Absalom stole the hearts of the men of Israel.
Abisalomu amachitira izi Aisraeli onse amene amabwera kwa mfumu kuti adzaweruzidwe ndipo Abisalomuyo anagwira mtima anthu a mu Israeli.
7 And it came to pass at the end of forty years, that Absalom said unto the king: 'I pray thee, let me go and pay my vow, which I have vowed unto the LORD, in Hebron.
Patapita zaka zinayi Abisalomu anati kwa mfumu, “Loleni ndipite ku Hebroni kuti ndikakwaniritse lonjezo limene ndinachita kwa Yehova.
8 For thy servant vowed a vow while I abode at Geshur in Aram, saying: If the LORD shall indeed bring me back to Jerusalem, then I will serve the LORD.'
Pamene mtumiki wanu amakhala ku Gesuri ku Aramu, anachita lonjezo ili: ‘Ngati Yehova adzandibweretsadi ku Yerusalemu, ndidzapembedza Yehovayo mu Hebroni.’”
9 And the king said unto him: 'Go in peace.' So he arose, and went to Hebron.
Mfumu inati kwa iye, “Pita mu mtendere” Kotero iye anapita ku Hebroni.
10 But Absalom sent spies throughout all the tribes of Israel, saying: 'As soon as ye hear the sound of the horn, then ye shall say: Absalom is king in Hebron.'
Ndipo Abisalomu anatuma amithenga ake mwamseri kwa mafuko onse a Israeli kukanena kuti, “Mukangomva kulira kwa malipenga pamenepo munene kuti, ‘Abisalomu ndiye mfumu mu Hebroni.’”
11 And with Absalom went two hundred men out of Jerusalem, that were invited, and went in their simplicity; and they knew not any thing.
Anthu 200 ochokera mu Yerusalemu anapita naye Abisalomu. Iwo anayitanidwa monga alendo ndipo anapita osadziwa chilichonse pa nkhaniyi.
12 And Absalom sent for Ahithophel the Gilonite, David's counsellor, from his city, even from Giloh, while he offered the sacrifices. And the conspiracy was strong; for the people increased continually with Absalom.
Pamene Abisalomu amapereka nsembe, iye anayitanitsanso Ahitofele Mgiloni, mlangizi wa Davide, wa ku Gilo, kotero kuwukiraku kunakula kwambiri, ndipo anthu otsatira Abisalomu anapitirira kuchuluka.
13 And there came a messenger to David, saying: 'The hearts of the men of Israel are after Absalom.'
Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”
14 And David said unto all his servants that were with him at Jerusalem: 'Arise, and let us flee; or else none of us shall escape from Absalom; make speed to depart, lest he overtake us quickly, and bring down evil upon us, and smite the city with the edge of the sword.'
Ndipo Davide anati kwa akuluakulu ake amene anali mu Yerusalemu. “Bwerani! Tiyeni tithawe, mwina palibe adzapulumuke kwa Abisalomu. Tiyeni tichoke msanga, mwina iye adzabwera msanga ndi kutipitirira, nʼkuwononga ife ndi mzinda wathu ndi lupanga.”
15 And the king's servants said unto the king: 'Behold, thy servants are ready to do whatsoever my lord the king shall choose.'
Akuluakulu a mfumu anamuyankha kuti, “Antchito anu ndi okonzeka kuchita chilichonse chimene mbuye wathu mfumu mukufuna kuchita.”
16 And the king went forth, and all his household after him. And the king left ten women, that were concubines, to keep the house.
Mfumu inanyamuka pamodzi ndi banja lake lonse. Koma iye anasiya azikazi khumi kuti azisamalira nyumba yaufumu.
17 And the king went forth, and all the people after him; and they tarried in Beth-merhak.
Kotero mfumu inanyamuka pamodzi ndi anthu onse oyitsatira, ndipo anayima pamalo pena chapatalipo.
18 And all his servants passed on beside him; and all the Cherethites, and all the Pelethites, and all the Gittites, six hundred men that came after him from Gath, passed on before the king.
Ankhondo ake onse anayamba kuyenda pamaso pa Davide, ndipo Akereti ndi Apeleti, pamodzinso ndi Agiti okwanira 600 amene anamutsata kuchokera ku Gati, nawonso anayenda pamaso pake.
19 Then said the king to Ittai the Gittite: 'Wherefore goest thou also with us? return, and abide with the king; for thou art a foreigner, and also an exile from thine own place.
Mfumu inati kwa Itai Mgiti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ukupita ndi ife? Bwerera ndipo ukakhale ndi mfumu Abisalomu. Iwe ndiwe mlendo munthu wothawa kwawo.
20 Whereas thou camest but yesterday, should I this day make thee go up and down with us, seeing I go whither I may? return thou, and take back thy brethren with thee in kindness and truth.'
Wangobwera dzulo lomweli, lero ndikutenge kuti uziyendayenda ndi ife, pamene ine sindikudziwa kumene ndikupita? Bwerera, ndipo tenga abale ako. Chifundo ndi kukhulupirika zikhale nawe.”
21 And Ittai answered the king, and said: 'As the LORD liveth, and as my lord the king liveth, surely in what place my lord the king shall be, whether for death or for life, even there also will thy servant be.'
Koma Itai anayankha mfumu kuti, “Pali Yehova wamoyo, kulikonse kumene mbuye wanga mfumu mudzakhala, kaya ndi moyo kapena imfa, mtumiki wanu adzakhala komweko.”
22 And David said to Ittai: 'Go and pass over.' And Ittai the Gittite passed over, and all his men, and all the little ones that were with him.
Davide anati kwa Itai, “Tiye pita nafe” Kotero Itai Mgiti anayenda pamodzi ndi anthu ake ndi mabanja amene anali naye.
23 And all the country wept with a loud voice, as all the people passed over; and as the king passed over the brook Kidron, all the people passed over, toward the way of the wilderness.
Anthu onse a madera ozungulira analira mofuwula pamene anthu onsewo amadutsa. Mfumunso inawoloka chigwa cha Kidroni, ndipo anthu onse anayenda kulowera ku chipululu.
24 And, lo, Zadok also came, and all the Levites with him, bearing the ark of the covenant of God; and they set down the ark of God — but Abiathar went up — until all the people had done passing out of the city.
Zadoki anali nawonso, ndipo Alevi onse amene anali naye ananyamula Bokosi la Chipangano la Mulungu. Iwo anayika pansi Bokosi la Mulungulo ndipo Abiatara ankapereka nsembe mpaka pamene anthu onse anamaliza kutuluka mu mzinda.
25 And the king said unto Zadok: 'Carry back the ark of God into the city; if I shall find favour in the eyes of the LORD, He will bring me back, and show me both it, and His habitation;
Kenaka mfumu inati kwa Zadoki, “Tenga Bokosi la Mulungu ubwerere nalo mu mzinda. Ngati ndidzapeza chifundo pamaso pa Yehova, adzandibweretsa kuti ndilionenso ndi malo ake okhalamo.
26 but if He say thus: I have no delight in thee; behold, here am I, let Him do to me as seemeth good unto Him.'
Koma iye anati, ‘Akapanda kukondwera nane,’ chabwino, andichite chimene chimukomere.”
27 The king said also unto Zadok the priest: 'Seest thou? return into the city in peace, and your two sons with you, Ahimaaz thy son, and Jonathan the son of Abiathar.
Mfumu inatinso kwa wansembe Zadoki, “Kodi siwe mlosi? Bwerera mu mzinda mwamtendere pamodzi ndi mwana wako Ahimaazi ndi Yonatani mwana wa Abiatara. Iwe ndi Abiatara tengani ana anu awiri.
28 See, I will tarry in the plains of the wilderness, until there come word from you to announce unto me.'
Ine ndidzadikira powolokera Yorodani ku chipululu mpaka nditalandira mawu ochokera kwa iwe ondiwuza mmene zilili zinthu.”
29 Zadok therefore and Abiathar carried the ark of God back to Jerusalem; and they abode there.
Kotero Zadoki ndi Abiatara ananyamula Bokosi la Mulungu lija nabwerera nalo ku Yerusalemu, ndipo anakakhala kumeneko.
30 And David went up by the ascent of the mount of Olives, and wept as he went up; and he had his head covered, and went barefoot; and all the people that were with him covered every man his head, and they went up, weeping as they went up.
Koma Davide anapitirira ndi kukakwera phiri la Olivi akupita nalira. Anafunda kumutu koma sanavale nsapato. Anthu onse amene anali naye anafundanso kumutu, ndipo nawonso amalira pamene amapita.
31 And one told David, saying: 'Ahithophel is among the conspirators with Absalom.' And David said: 'O LORD, I pray Thee, turn the counsel of Ahithophel into foolishness.'
Tsono Davide anamva kuti, “Ahitofele ali pakati pa anthu owukira pamodzi ndi Abisalomu.” Choncho Davide anapemphera, “Inu Yehova, musandutse uphungu wa Ahitofele ukhale uchitsiru.”
32 And it came to pass, that when David was come to the top of the ascent, where God was wont to be worshipped, behold, Hushai the Archite came to meet him with his coat rent, and earth upon his head.
Davide atafika pamwamba pa phiri pomwe anthu ankapembedzerapo Mulungu, Husai Mwariki anadzakumana naye atangʼamba mkanjo wake ndi kudzithira fumbi kumutu.
33 And David said unto him: 'If thou passest on with me, then thou wilt be a burden unto Me;
Davide anati kwa iye, “Ngati iwe upite ndi ine, udzakhala chondilemetsa.
34 but if thou return to the city, and say unto Absalom: I will be thy servant, O king; as I have been thy father's servant in time past, so will I now be thy servant; then wilt thou defeat for me the counsel of Ahithophel.
Koma ngati ubwerera ku mzinda ndi kukanena kwa Abisalomu kuti, ‘Inu mfumu ine ndidzakhala wantchito wanu.’ Mʼmbuyomu ndinali wantchito wa abambo anu koma tsopano ndidzakhala wantchito wanu. Ukatero udzandithandiza kulepheretsa malangizo a Ahitofele.
35 And hast thou not there with thee Zadok and Abiathar the priests? therefore it shall be, that what thing soever thou shalt hear out of the king's house, thou shalt tell it to Zadok and Abiathar the priests.
Kodi ansembe, Zadoki ndi Abiatara, sakukhala nawe kumeneko? Ukawawuze zonse zimene umamva mʼnyumba yaufumu.
36 Behold, they have there with them their two sons, Ahimaaz Zadok's son, and Jonathan Abiathar's son; and by them ye shall send unto me every thing that ye shall hear.'
Ana awo awiri, Ahimaazi wa Zadoki, ndi Yonatani mwana wa Abiatara ali nawo pamodzi, uzikawatuma kwa ine ndi china chilichonse chimene ukamve.”
37 So Hushai David's friend came into the city; and Absalom was at the point of coming into Jerusalem.
Ndipo Husai bwenzi la Davide anafika ku Yerusalemu pamene Abisalomu amalowa mu mzinda.

< 2 Samuel 15 >