< Luke 3 >

1 NOW in the fifteenth year of the reign of Tiberius Caesar, Pontius Pilate being governor of Judea, and Herod tetrarch of Galilee, and Philip his brother tetrarch of Iturea and the region of Trachonitis, and Lysanias tetrarch of Abilene:
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 when Annas and Caiaphas were high-priests, the word of God came to John the son of Zacharias in the wilderness;
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 and he came into all the country on the confines of Jordan, preaching the baptism of repentance for the remission of sins;
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 as it is written in the book of the words of the prophet Isaiah, saying, “The voice of one crying in the wilderness, Prepare ye the way of the Lord, make his paths strait:
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 every valley shall be filled up, and every mountain and hill shall be levelled, and the crooked ways made strait, and the rough roads smooth:
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 and all flesh shall see the salvation of God.”
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 He said, therefore, to the multitudes who came out to be baptised by him, Ye broods of vipers, who hath warned you to fly from the approaching wrath?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 Produce then fruits worthy of repentance, and begin not to say in yourselves, We have a father, even Abraham; for I say unto you, That God is able out of these stones to raise up children to Abraham.
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 But now is the ax laid even to the root of the trees; every tree therefore that produceth not good fruit, is cut down and cast into the fire.
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 And the multitudes asked him, saying, What then shall we do?
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 And he answering said to them, He that hath two coats, let him give to him that hath none; and he that hath provisions, let him do in like manner.
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 Then came also the farmers of the taxes to be baptised, and they said unto him, Master, what shall we do?
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 He said unto them, Exact nothing more than is appointed for you.
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 And the military men also asked him, And what shall we do? And he said unto them, Extort nothing by force; nor turn informers; and be content with your pay.
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 Now when the people were in expectation, and many reasoned in their hearts respecting John, whether he were the Messiah,
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 John addressed himself to them all, saying, I indeed baptise you with water; but one mightier than I is coming, the thong of whose sandals I am not worthy to untie: he shall baptise you with the Holy Ghost and with fire;
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 whose winnowing fan is in his hand, and he will thoroughly cleanse his threshing-floor, and collect the wheat into his granary; but the chaff he will burn with fire unquenchable.
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 Thus in many and various discourses exhorting them, he preached the glad tidings of the gospel to the people.
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 Now Herod the tetrarch, being reproved by him, on account of Herodias his brother Philip’s wife, and for all the other wicked actions which he had done,
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 added this also to all the rest, and shut up John in prison.
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 Now it came to pass, at the time when John was baptising all the people, that Jesus also was baptised, and as he prayed, the heaven was opened,
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 and the Holy Ghost descended in a bodily form, like a dove, upon him, and a voice came from heaven, saying, Thou art my beloved Son, in thee I am well pleased.
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 And Jesus himself was about thirty years of age when he began his ministry, being (as was supposed the son of Joseph) of Heli,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 of Matthat, of Levi, of Melchi, of Janna, of Joseph,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 of Mattathias, of Amos, of Naum, of Esli, of Nagge,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 of Maath, of Mattathias, of Semei, of Joseph, of Juda,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 of Joanna, of Rhesa, of Zerubbabel, of Salathiel, of Neri,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 of Melchi, of Addi, of Cosam, of Elmodam, of Er,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 of Jose, of Eliezer, of Jorim, of Matthat, of Levi,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 of Simeon, of Judah, of Joseph, of Jonan, of Eliakim,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 of Melea, of Menan, of Mattatha, of Nathan, of David,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 of Jesse, of Obed, of Booz, of Salmon, of Naasson,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 of Aminadab, of Aram, of Esrom, of Phares, of Judah,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 of Jacob, of Isaac, of Abraham, of Terah, of Nachor,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 of Saruch, of Ragau, of Phalec, of Heber, of Sala,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 of Cainan, of Arphaxad, of Sem, of Noe, of Lamech,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 of Methusaleh, of Enoch, of Jared, of Maleleel, of Cainan,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 of Enos, of Seth, of Adam, the son of God.
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< Luke 3 >