< Romans 1 >

1 Paul a seruant of Iesus Christ called to be an Apostle, put apart to preache the Gospel of God,
Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
2 (Which he had promised afore by his Prophetes in the holy Scriptures)
umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
3 Concerning his Sonne Iesus Christ our Lord (which was made of the seede of Dauid according to the flesh,
Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
4 And declared mightily to be the Sonne of God, touching the Spirit of sanctification by the resurrection from the dead)
Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
5 By whom we haue receiued grace and Apostleship (that obedience might be giuen vnto ye faith) for his Name among al ye Gentiles,
ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
6 Among whom ye be also the called of Iesus Christ:
Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7 To all you that be at Rome beloued of God, called to be Saints: Grace be with you, and peace from God our Father, and from the Lord Iesus Christ.
Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
8 First I thanke my God through Iesus Christ for you all, because your faith is published throughout the whole world.
Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
9 For God is my witnesse (whom I serue in my spirit in the Gospel of his Sonne) that without ceasing I make mention of you
Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
10 Alwayes in my prayers, beseeching that by some meanes, one time or other I might haue a prosperous iourney by the will of God, to come vnto you.
Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11 For I long to see you, that I might bestowe among you some spirituall gift, that you might be strengthened:
Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
12 That is, that I might be comforted together with you, through our mutuall faith, both yours and mine.
ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
13 Now my brethren, I would that ye should not be ignorant, how that I haue oftentimes purposed to come vnto you (but haue bene let hitherto) that I might haue some fruite also among you, as I haue among the other Gentiles.
Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14 I am detter both to the Grecians, and to the Barbarians, both to the wise men and vnto the vnwise.
Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
15 Therefore, as much as in me is, I am readie to preach ye Gospel to you also that are at Rome.
Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16 For I am not ashamed of the Gospel of Christ: for it is the power of God vnto saluation to euery one that beleeueth, to the Iewe first, and also to the Grecian.
Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
17 For by it the righteousnesse of God is reueiled from faith to faith: as it is written, The iust shall liue by faith.
Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
18 For the wrath of God is reueiled from heauen against all vngodlinesse, and vnrighteousnesse of men, which withhold the trueth in vnrighteousnesse.
Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
19 Forasmuch as that, which may be knowe of God, is manifest in them: for God hath shewed it vnto them.
Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
20 For the inuisible things of him, that is, his eternal power and Godhead, are seene by ye creation of the worlde, being considered in his workes, to the intent that they should be without excuse: (aïdios g126)
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios g126)
21 Because that when they knewe God, they glorified him not as God, neither were thankefull, but became vaine in their thoughtes, and their foolish heart was full of darkenesse.
Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
22 When they professed themselues to be wise, they became fooles.
Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
23 For they turned the glorie of the incorruptible God to the similitude of the image of a corruptible man, and of birdes, and foure footed beastes, and of creeping things.
Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 Wherefore also God gaue them vp to their hearts lusts, vnto vncleannesse, to defile their owne bodies betweene themselues:
Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
25 Which turned the trueth of God vnto a lie, and worshipped and serued the creature, forsaking the Creator, which is blessed for euer, Amen. (aiōn g165)
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
26 For this cause God gaue them vp vnto vile affections: for euen their women did change the naturall vse into that which is against nature.
Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
27 And likewise also the men left the naturall vse of the woman, and burned in their lust one toward another, and man with man wrought filthinesse, and receiued in themselues such recompence of their errour, as was meete.
Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28 For as they regarded not to acknowledge God, euen so God deliuered them vp vnto a reprobate minde, to doe those things which are not conuenient,
Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
29 Being full of all vnrighteousnesse, fornication, wickednes, couetousnes, maliciousnes, full of enuie, of murder, of debate, of deceit, taking all things in the euill part, whisperers,
Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
30 Backbiters, haters of God, doers of wrong, proude, boasters, inuenters of euil things, disobedient to parents,
osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
31 without vnderstanding, couenant breakers, without naturall affection, such as can neuer be appeased, mercilesse.
alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
32 Which men, though they knew ye Lawe of God, how that they which comit such things are worthie of death, yet not onely do the same, but also fauour them that doe them.
Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.

< Romans 1 >