< Psalms 92 >

1 A Psalme or song for the Sabbath day. It is a good thing to praise the Lord, and to sing vnto thy Name, O most High,
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 To declare thy louing kindenesse in the morning, and thy trueth in the night,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 Vpon an instrument of tenne strings, and vpon the viole with the song vpon the harpe.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 For thou, Lord, hast made mee glad by thy workes, and I wil reioyce in the workes of thine handes.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 O Lord, how glorious are thy workes! and thy thoughtes are very deepe.
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 An vnwise man knoweth it not, and a foole doeth not vnderstand this,
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 (When the wicked growe as the grasse, and all the workers of wickednesse doe flourish) that they shall be destroyed for euer.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 But thou, O Lord, art most High for euermore.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 For loe, thine enemies, O Lord: for loe, thine enemies shall perish: all the workers of iniquitie shall be destroyed.
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 But thou shalt exalt mine horne, like the vnicornes, and I shalbe anoynted with fresh oyle.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Mine eye also shall see my desire against mine enemies: and mine eares shall heare my wish against the wicked, that rise vp against me.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 The righteous shall flourish like a palme tree, and shall grow like a Cedar in Lebanon.
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 Such as bee planted in the house of the Lord, shall flourish in the courtes of our God.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 They shall still bring foorth fruite in their age: they shall be fat and flourishing,
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 To declare that the Lord my rocke is righteous, and that none iniquitie is in him.
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Psalms 92 >