< Psalms 8 >

1 To him that excelleth on Gittith. A Psalme of Dauid. O Lord our Lord, how excellent is thy Name in all the worlde! which hast set thy glory aboue the heauens.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
2 Out of the mouth of babes and suckelings hast thou ordeined strength, because of thine enemies, that thou mightest still the enemie and the auenger.
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 When I beholde thine heauens, euen the workes of thy fingers, the moone and the starres which thou hast ordeined,
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
4 What is man, say I, that thou art mindefull of him? and the sonne of man, that thou visitest him?
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 For thou hast made him a little lower then God, and crowned him with glory and worship.
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 Thou hast made him to haue dominion in the workes of thine hands: thou hast put all things vnder his feete:
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 All sheepe and oxen: yea, and the beastes of the fielde:
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
8 The foules of the ayre, and the fish of the sea, and that which passeth through the paths of the seas.
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 O Lord our Lord, howe excellent is thy Name in all the world!
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< Psalms 8 >