< Psalms 35 >

1 A Psalme of Dauid. Pleade thou my cause, O Lord, with them that striue with me: fight thou against them, that fight against me.
Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
2 Lay hand vpon the shielde and buckler, and stand vp for mine helpe.
Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
3 Bring out also the speare and stop the way against them, that persecute me: say vnto my soule, I am thy saluation.
Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
4 Let them be confounded and put to shame, that seeke after my soule: let them be turned backe, and brought to confusion, that imagine mine hurt.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
5 Let them be as chaffe before the winde, and let the Angel of the Lord scatter them.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
6 Let their way be darke and slipperie: and let the Angel of the Lord persecute them.
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
7 For without cause they haue hid the pit and their net for me: without cause haue they digged a pit for my soule.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
8 Let destruction come vpon him at vnwares, and let his net, that he hath laid priuilie, take him: let him fall into the same destruction.
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
9 Then my soule shalbe ioyfull in the Lord: it shall reioyce in his saluation.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 All my bones shall say, Lord, who is like vnto thee, which deliuerest the poore from him, that is too strong for him! yea, the poore and him that is in miserie, from him that spoyleth him!
Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
11 Cruell witnesses did rise vp: they asked of me things that I knewe not.
Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 They rewarded me euill for good, to haue spoyled my soule.
Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 Yet I, when they were sicke, I was clothed with a sacke: I humbled my soule with fasting: and my praier was turned vpon my bosome.
Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14 I behaued my selfe as to my friend, or as to my brother: I humbled my selfe, mourning as one that bewaileth his mother.
ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 But in mine aduersitie they reioyced, and gathered them selues together: the abiects assembled themselues against me, and knewe not: they tare me and ceased not,
Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 With the false skoffers at bankets, gnashing their teeth against me.
Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
17 Lord, how long wilt thou beholde this? deliuer my soule from their tumult, euen my desolate soule from the lions.
Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
18 So will I giue thee thankes in a great Congregation: I will praise thee among much people.
Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
19 Let not them that are mine enemies, vniustly reioyce ouer mee, neyther let them winke with the eye, that hate mee without a cause.
Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 For they speake not as friendes: but they imagine deceitfull woordes against the quiet of the lande.
Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 And they gaped on mee with their mouthes, saying, Aha, aha, our eye hath seene.
Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
22 Thou hast seene it, O Lord: keepe not silence: be not farre from me, O Lord.
Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Arise and wake to my iudgement, euen to my cause, my God, and my Lord.
Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Iudge me, O Lord my God, according to thy righteousnesse, and let them not reioyce ouer mee.
Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 Let them not say in their hearts, O our soule reioyce: neither let them say, We haue deuoured him.
Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
26 Let them bee confounded, and put to shame together, that reioyce at mine hurt: let them bee clothed with confusion and shame, that lift vp themselues against me.
Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 But let them be ioyful and glad, that loue my righteousnesse: yea, let them say alway, Let the Lord be magnified, which loueth the prosperitie of his seruant.
Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 And my tongue shall vtter thy righteousnesse, and thy praise euery day.
Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.

< Psalms 35 >