< Psalms 145 >

1 A Psalme of David of Praise. O my God and King, I will extold thee, and will blesse thy Name for euer and euer.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 I will blesse thee dayly, and prayse thy Name for euer and euer.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Great is the Lord, and most worthy to be praysed, and his greatnes is incomprehensible.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Generation shall praise thy works vnto generation, and declare thy power.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 I wil meditate of the beautie of thy glorious maiestie, and thy wonderfull workes,
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 And they shall speake of the power of thy fearefull actes, and I will declare thy greatnes.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 They shall breake out into the mention of thy great goodnes, and shall sing aloude of thy righteousnesse.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 The Lord is gracious and merciful, slow to anger, and of great mercie.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 The Lord is good to all, and his mercies are ouer all his workes.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 All thy workes prayse thee, O Lord, and thy Saints blesse thee.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 They shewe the glory of thy kingdome, and speake of thy power,
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 To cause his power to be knowen to the sonnes of men, and the glorious renoume of his kingdome.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Thy kingdome is an euerlasting kingdome, and thy dominion endureth throughout all ages.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 The Lord vpholdeth all that fall, and lifteth vp all that are ready to fall.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 The eyes of all waite vpon thee, and thou giuest them their meate in due season.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Thou openest thine hand, and fillest all things liuing of thy good pleasure.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 The Lord is righteous in all his wayes, and holy in all his workes.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 The Lord is neere vnto all that call vpon him: yea, to all that call vpon him in trueth.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 He wil fulfill the desire of them that feare him: he also wil heare their cry, and wil saue them.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 The Lord preserueth all them that loue him: but he will destroy all the wicked.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 My mouth shall speake the prayse of the Lord, and all flesh shall blesse his holy Name for euer and euer.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Psalms 145 >