< Psalms 125 >

1 A song of degrees. They that trust in the Lord, shalbe as mount Zion, which can not be remooued, but remaineth for euer.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 As the mountaines are about Ierusalem: so is the Lord about his people from henceforth and for euer.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 For the rod of the wicked shall not rest on the lot of the righteous, least the righteous put forth their hand vnto wickednes.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Doe well, O Lord, vnto those that be good and true in their hearts.
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 But these that turne aside by their crooked wayes, them shall the Lord leade with the workers of iniquitie: but peace shalbe vpon Israel.
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.

< Psalms 125 >