< Psalms 113 >

1 Praise ye the Lord. Praise, O ye seruants of the Lord, prayse the Name of the Lord.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Blessed be the Name of the Lord from hencefoorth and for euer.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 The Lordes Name is praysed from the rising of ye sunne, vnto ye going downe of the same.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 The Lord is high aboue all nations, and his glorie aboue the heauens.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Who is like vnto the Lord our God, that hath his dwelling on high!
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 Who abaseth himselfe to beholde things in the heauen and in the earth!
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 He raiseth the needie out of the dust, and lifteth vp the poore out of the dung,
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 That he may set him with the princes, euen with the princes of his people.
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 He maketh the barren woman to dwell with a familie, and a ioyfull mother of children. Prayse ye the Lord.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalms 113 >