< Psalms 102 >

1 A prayer of the afflicted, when he shall be in distresse, and pour forth his meditation before the Lord. O Lord, heare my prayer, and let my crye come vnto thee.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Hide not thy face from me in the time of my trouble: incline thine eares vnto me: when I call, make haste to heare me.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 For my dayes are consumed like smoke, and my bones are burnt like an herthe.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Mine heart is smitten and withereth like grasse, because I forgate to eate my bread.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 For the voyce of my groning my bones doe cleaue to my skinne.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 I am like a pelicane of the wildernesse: I am like an owle of the deserts.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 I watch and am as a sparrowe alone vpon the house top.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Mine enemies reuile me dayly, and they that rage against me, haue sworne against me.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Surely I haue eaten asshes as bread, and mingled my drinke with weeping,
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 Because of thine indignation and thy wrath: for thou hast heaued me vp, and cast me downe.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 My dayes are like a shadowe that fadeth, and I am withered like grasse.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 But thou, O Lord, doest remaine for euer, and thy remembrance from generation to generation.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Thou wilt arise and haue mercy vpon Zion: for the time to haue mercie thereon, for the appointed time is come.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 For thy seruants delite in the stones thereof, and haue pitie on the dust thereof.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Then the heathen shall feare the Name of the Lord, and all the Kings of the earth thy glory,
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 When the Lord shall build vp Zion, and shall appeare in his glory,
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 And shall turne vnto the prayer of the desolate, and not despise their prayer.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 This shall be written for the generation to come: and the people, which shalbe created, shall prayse the Lord.
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 For he hath looked downe from the height of his Sanctuarie: out of the heauen did the Lord beholde the earth,
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 That he might heare the mourning of the prisoner, and deliuer the children of death:
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 That they may declare the Name of the Lord in Zion, and his prayse in Ierusalem,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 When the people shalbe gathered together, and the kingdomes to serue the Lord.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 He abated my strength in the way, and shortened my dayes.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 And I sayd, O my God, take me not away in the middes of my dayes: thy yeeres endure from generation to generation.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Thou hast aforetime layde the foundation of the earth, and the heauens are the worke of thine hands.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 They shall perish, but thou shalt endure: euen they all shall waxe olde as doeth a garment: as a vesture shalt thou change them, and they shall be changed.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 But thou art the same, and thy yeeres shall not fayle.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 The children of thy seruants shall continue, and their seede shall stand fast in thy sight.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Psalms 102 >