< Leviticus 5 >

1 Also if any haue sinned, that is, If he haue heard the voyce of an othe, and hee can be a witnes, whether he hath seene or knowen of it, if hee doe not vtter it, he shall beare his iniquitie:
“‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
2 Either if one touche any vncleane thing, whether it be a carion of an vncleane beast, or a carion of vncleane cattel, or a carion of vncleane creeping things, and is not ware of it, yet he is vncleane, and hath offended:
“‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
3 Eyther if hee touche any vncleannesse of man (whatsoeuer vncleannes it be, that hee is defiled with) and is not ware of it, and after commeth to the knowledge of it, he hath sinned:
“‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
4 Either if any sweare and pronounce with his lippes to do euill, or to doe good (whatsoeuer it bee that a man shall pronounce with an othe) and it be hid from him, and after knoweth that he hath offended in one of these poyntes,
“‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
5 Whe he hath sinned in any of these things, then he shall confesse that he hath sinned therein.
“‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
6 Therefore shall he bring his trespasse offring vnto the Lord for his sinne which he hath committed, euen a female from ye flocke, be it a lambe or a she goat for a sinne offring, and the Priest shall make an atonement for him, concerning his sinne.
Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
7 But if he be not able to bring a sheepe, he shall bring for his trespas which he hath committed, two turtle doues, or two yong pigeons vnto the Lord, one for a sinne offring, and the other for a burnt offring.
“‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
8 So he shall bring them vnto the Priest, who shall offer the sinne offring first, and wring the necke of it a sunder, but not plucke it cleane off.
Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
9 After he shall sprinkle of the blood of the sinne offring vpon the side of the altar, and the rest of the blood shall be shed at the foote of the altar: for it is a sinne offering.
kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
10 Also he shall offer the seconde for a burnt offring as the maner is: so shall the Priest make an atonement for him (for his sinne which hee hath committed) and it shalbe forgiuen him.
Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
11 But if he be not able to bring two turtle doues, or two yong pigeons, then he that hath sinned, shall bring for his offring, the tenth parte of an Ephah of fine floure for a sinne offring, he shall put none oyle thereto, neither put any incense thereon: for it is a sinne offering.
“‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
12 Then shall hee bring it to the Priest, and the Priest shall take his handfull of it for the remembrance thereof, and burne it vpon the altar with the offrings of the Lord made by fire: for it is a sinne offring.
Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
13 So the Priest shall make an atonement for him, as touching his sinne that he hath committed in one of these poyntes, and it shall bee forgiuen him: and the remnant shalbe the Priests, as the meate offring.
Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
14 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
15 If any person transgresse and sinne through ignorance by taking away things consecrated vnto the Lord, hee shall then bring for his trespasse offring vnto the Lord a ramme without blemish out of the flocke, worth two shekels of siluer by thy estimation after the shekel of the Sanctuarie, for a trespasse offring.
“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
16 So hee shall restore that wherein hee hath offended, in taking away of the holy thing, and shall put the fift part more thereto, and giue it vnto the Priest: so the Priest shall make an atonement for him with the ram of ye trespasse offring, and it shalbe forgiuen him.
Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
17 Also if any sinne and doe against any of the commandements of the Lord, which ought not to be done, and knowe not and sinne and beare his iniquitie,
“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
18 Then shall he bring a ramme without blemishe out of the flocke, in thy estimation worth two shekels for a trespasse offring vnto ye Priest: and the Priest shall make an atonement for him concerning his ignorance wherein he erred, and was not ware: so it shalbe forgiuen him.
Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
19 This is the trespasse offring for the trespasse committed against the Lord.
Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”

< Leviticus 5 >