< Judges 20 >

1 Then all the children of Israel went out, and the Congregation was gathered together as one man, from Dan to Beersheba, with the land of Gilead, vnto the Lord in Mizpeh.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
2 And the chiefe of all the people, and all the tribes of Israel assembled in the Congregation of the people of God foure hundreth thousand footemen that drewe sword.
Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
3 (Now the children of Beniamin heard that the children of Israel were gone vp to Mizpeh) Then the children of Israel saide, Howe is this wickednesse committed?
Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
4 And the same Leuite, the womans husband that was slaine, answered and saide, I came vnto Gibeah that is in Beniamin with my concubine to lodge,
Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
5 And the men of Gibeah arose against me, and beset the house round about vpon mee by night, thinking to haue slaine me, and haue forced my concubine that she is dead.
Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
6 Then I tooke my concubine, and cut her in pieces, and sent her throughout all the countrey of the inheritance of Israel: for they haue committed abomination and villenie in Israel.
Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
7 Behold, ye are al children of Israel: giue your aduise, and counsell herein.
Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
8 Then all the people arose as one man, saying, There shall not a man of vs goe to his tent, neither any turne into his house.
Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
9 But now this is that thing which we will do to Gibeah: we wil goe vp by lot against it,
Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
10 And we wil take ten men of the hundreth throughout al the tribes of Israel, and an hundreth of the thousand, and a thousand of ten thousand to bring vitaile for the people that they may do (when they come to Gibeah of Beniamin) according to all the villeny, that it hath done in Israel.
Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
11 So all the men of Israel were gathered against the citie, knit together, as one man.
Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
12 And the tribes of Israel sent men through al the tribe of Beniamin, saying, What wickednesse is this that is committed among you?
Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
13 Nowe therefore deliuer vs those wicked men which are in Gibeah, that we may put them to death, and put away euill from Israel: but the children of Beniamin would not obey the voyce of their brethren the children of Israel.
Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
14 But ye children of Beniamin gathered them selues together out of the cities vnto Gibeah, to come out and fight against the children of Israel.
Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
15 And ye children of Beniamin were nombred at that time out of the cities sixe and twenty thousand men that drewe sworde, beside the inhabitants of Gibeah, which were nombred seuen hundreth chosen men.
Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
16 Of all this people were seuen hundreth chosen men, being left handed: all these could sling stones at an heare breadth, and not faile.
Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
17 Also the men of Israel, beside Beniamin, were nombred foure hundreth thousande men that drew sword, euen all men of warre.
Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
18 And the children of Israel arose, and went vp to the house of God, and asked of God, saying, Which of vs shall goe vp first to fight against the children of Beniamin? And the Lord said, Iudah shalbe first.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
19 Then the children of Israel arose vp earely and camped against Gibeah.
Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
20 And the men of Israel went out to battell against Beniamin, and the men of Israel put themselues in aray to fight against the beside Gibeah.
Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
21 And the children of Beniamin came out of Gibeah, and slewe downe to the ground of the Israelites that day two and twentie thousand men.
A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
22 And the people, the men of Israel plucked vp their hearts, and set their battel againe in aray in the place where they put them in aray the first day.
Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
23 (For the children of Israel had gone vp and wept before the Lord vnto the euening, and had asked of the Lord, saying, Shall I goe againe to battel against the children of Beniamin my brethren? and the Lord said, Go vp against them)
Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
24 Then the children of Israel came neere against the children of Beniamin the second day.
Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
25 Also the second day Beniamin came forth to meete them out of Gibeah, and slewe downe to the grounde of the children of Israel againe eighteene thousand men: all they could handle the sword.
Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
26 Then al the children of Israel went vp and all the people came also vnto the house of God, and wept and sate there before the Lord and fasted that day vnto the euening, and offred burnt offrings and peace offrings before the Lord.
Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
27 And the children of Israel asked the Lord (for there was the Arke of the couenat of God in those dayes,
Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
28 And Phinehas the sonne of Eleazar, the sonne of Aaron stoode before it at that time) saying, Shall I yet goe anie more to battel against the children of Beniamin my brethren, or shall I cease? And the Lord said, Go vp: for to morowe I will deliuer them into your hand.
Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
29 And Israel set men to lie in waite round about Gibeah.
Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
30 And the children of Israel went vp against the children of Beniamin the third day, and put theselues in aray against Gibeah, as at other times.
Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
31 Then the children of Beniamin comming out against the people, were drawen from the citie: and they began to smite of ye people and kill as at other times, euen by the wayes in the fielde (whereof one goeth vp to the house of God, and the other to Gibeah) vpon a thirtie men of Israel.
Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
32 (For the children of Beniamin sayd, They are fallen before vs, as at the first. But the children of Israel saide, Let vs flee and plucke them away from the citie vnto the hie wayes)
Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
33 And all the men of Israel rose vp out of their place, and put themselues in aray at Baal-tamar: and the men that lay in wayte of the Israelites came forth of their place, euen out of the medowes of Gibeah,
Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
34 And they came ouer against Gibeah, ten thousande chosen men of all Israel, and the battell was sore: for they knewe not that the euill was neere them.
Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
35 And the Lord smote Beniamin before Israel, and the children of Israel destroyed of the Beniamites the same day fiue and twenty thousand and an hundreth men: all they could handle the sword.
Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
36 So the children of Beniamin sawe that they were striken downe: for the men of Israel gaue place to the Beniamites, because they trusted to the men that lay in waite, which they had laide beside Gibeah.
Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
37 And they that lay in wait hasted, and brake forth toward Gibeah, and the ambushment drewe themselues along, and smote all the citie with the edge of the sword.
Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
38 Also the men of Israel had appoynted a certaine time with the ambushmentes, that they should make a great flame and smoke rise vp out of the citie.
Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
39 And when the men of Israel retired in the battel, Beniamin began to smite and kill of the men of Israel about thirtie persons: for they said, Surely they are striken downe before vs, as in the first battell.
ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
40 But when the flame bega to arise out of the citie, as a pillar of smoke, the Beniamites looked backe, and behold, the flame of the citie began to ascend vp to heauen.
Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
41 Then the men of Israel turned againe, and the men of Beniamin were astonied: for they saw that euill was neere vnto them.
Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
42 Therefore they fled before the men of Israel vnto the way of the wildernesse, but the battell ouertooke them: also they which came out of the cities, slew them among them.
Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
43 Thus they compassed the Beniamites about, and chased them at ease, and ouerranne them, euen ouer against Gibeah on the Eastside.
Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
44 And there were slaine of Beniamin eyghteene thousad men, which were all men of warre.
Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
45 And they turned and fled to the wildernes vnto the rocke of Rimmon: and the Israelites glayned of them by the way fiue thousand men, and pursued after them vnto Gidom, and slewe two thousand men of them,
Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
46 So that all that were slayne that day of Beniamin, were fiue and twentie thousand men that drewe sword, which were all men of warre:
Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
47 But sixe hundreth men turned and fled to the wildernesse vnto the rocke of Rimmon, and abode in the rocke of Rimmon foure moneths.
Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
48 Then the men of Israel returned vnto the children of Beniamin, and smote them with the edge of the sword from the men of the citie vnto the beasts, and all that came to hand: also they set on fire all the cities that they coulde come by.
Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.

< Judges 20 >