< Job 31 >

1 I made a couenant with mine eyes: why then should I thinke on a mayde?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 For what portion should I haue of God from aboue? and what inheritance of the Almightie from on hie?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Is not destruction to the wicked and strange punishment to the workers of iniquitie?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Doeth not he beholde my wayes and tell all my steps?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 If I haue walked in vanitie, or if my foote hath made haste to deceite,
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Let God weigh me in the iust balance, and he shall know mine vprightnes.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 If my steppe hath turned out of the way, or mine heart hath walked after mine eye, or if any blot hath cleaued to mine handes,
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Let me sowe, and let another eate: yea, let my plantes be rooted out.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 If mine heart hath bene deceiued by a woman, or if I haue layde wayte at the doore of my neighbour,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Let my wife grinde vnto another man, and let other men bow downe vpon her:
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 For this is a wickednes, and iniquitie to bee condemned:
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Yea, this is a fire that shall deuoure to destruction, and which shall roote out al mine increase,
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 If I did contemne the iudgement of my seruant, and of my mayde, when they did contend with me,
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 What then shall I do when God standeth vp? and when he shall visit me, what shall I answere?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 He that hath made me in the wombe, hath he not made him? hath not he alone facioned vs in the wombe?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 If I restrained the poore of their desire, or haue caused the eyes of the widow to faile,
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Or haue eaten my morsels alone, and the fatherles hath not eaten thereof,
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 (For from my youth hee hath growen vp with me as with a father, and from my mothers wombe I haue bene a guide vnto her)
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 If I haue seene any perish for want of clothing, or any poore without couering,
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 If his loynes haue not blessed me, because he was warmed with the fleece of my sheepe,
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 If I haue lift vp mine hande against the fatherlesse, when I saw that I might helpe him in the gate,
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Let mine arme fal from my shoulder, and mine arme be broken from the bone.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 For Gods punishment was fearefull vnto me, and I could not be deliuered from his highnes.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 If I made gold mine hope, or haue sayd to the wedge of golde, Thou art my confidence,
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 If I reioyced because my substance was great, or because mine hand had gotten much,
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 If I did behold the sunne, when it shined, or the moone, walking in her brightnes,
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 If mine heart did flatter me in secrete, or if my mouth did kisse mine hand,
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 (This also had bene an iniquitie to be condemned: for I had denied the God aboue)
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 If I reioyced at his destruction that hated me, or was mooued to ioye when euill came vpon him,
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Neither haue I suffred my mouth to sinne, by wishing a curse vnto his soule.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 Did not the men of my Tabernacle say, Who shall giue vs of his flesh? we can not bee satisfied.
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 The stranger did not lodge in the streete, but I opened my doores vnto him, that went by the way.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 If I haue hid my sinne, as Adam, concealing mine iniquitie in my bosome,
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 Though I could haue made afraid a great multitude, yet the most contemptible of the families did feare me: so I kept silence, and went not out of the doore.
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Oh that I had some to heare me! beholde my signe that the Almightie will witnesse for me: though mine aduersary should write a booke against me,
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Woulde not I take it vpon my shoulder, and binde it as a crowne vnto me?
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 I will tell him the nomber of my goings, and goe vnto him as to a prince.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 If my lande cry against me, or the furrowes thereof complayne together,
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 If I haue eaten the fruites thereof without siluer: or if I haue grieued the soules of the masters thereof,
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Let thistles growe in steade of wheate, and cockle in the stead of Barley. The wordes of Iob are ended.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >