< Jeremiah 6 >

1 O ye children of Beniamin, prepare to flee out of the middes of Ierusalem, and blowe the trumpet in Tekoa: set vp a standart vpon Beth-haccerem: for a plague appeareth out of the North and great destruction.
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 I haue compared the daughter of Zion to a beautifull and daintie woman.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 The pastors with their flockes shall come vnto her: they shall pitche their tentes rounde about by her, and euery one shall feede in his place.
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 Prepare warre against her: arise, and let vs goe vp toward the South: wo vnto vs: for the day declineth, and the shadowes of the euening are stretched out.
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 Arise, and let vs goe vp by night, and destroy her palaces.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 For thus hath the Lord of hostes said, Hewe downe wood, and cast a mounte against Ierusalem: this citie must be visited: all oppression is in the middes of it.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 As the fountaine casteth out her waters, so she casteth out her malice: crueltie and spoyle is continually heard in her before me with sorowe and strokes.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Be thou instructed, O Ierusalem, lest my soule depart from thee, lest I make thee desolate as a land, that none inhabiteth.
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Thus sayeth the Lord of hostes, They shall gather as a vine, the residue of Israel: turne backe thine hande as the grape gatherer into the baskets.
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 Vnto whome shall I speake, and admonish that they may heare? beholde, their eares are vncircumcised, and they cannot hearken: beholde, the worde of the Lord is vnto them as a reproche: they haue no delite in it.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 Therefore I am full of the wrath of the Lord: I am weary with holding it: I will powre it out vpon the children in the streete, and likewise vpon the assembly of the yong men: for the husband shall euen be taken with the wife, and the aged with him that is full of daies.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 And their houses with their landes, and wiues also shalbe turned vnto strangers: for I will stretch out mine hande vpon the inhabitants of the land, sayeth the Lord.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 For from the least of them, euen vnto the greatest of them, euery one is giuen vnto couetousnesse, and from the Prophet euen vnto the Priest, they all deale falsely.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 They haue healed also ye hurt of the daughter of my people with sweete woordes, saying, Peace, peace, when there is no peace.
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Were they ashamed when they had committed abomination? nay, they were not ashamed, no neither coulde they haue any shame: therefore they shall fall among the slaine: when I shall visite them, they shall be cast downe, sayth the Lord.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Thus sayeth the Lord, Stande in the waies and beholde, and aske for the olde way, which is the good way and walke therein, and yee shall finde rest for your soules: but they saide, We will not walke therein.
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 Also I set watchmen ouer you, which said, Take heede to the sound of the trumpet: but they said, We will not take heede.
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 Heare therefore, yee Gentiles, and thou Congregation knowe, what is among them.
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Heare, O earth, beholde, I will cause a plague to come vpon this people, euen the fruite of their owne imaginations: because they haue not taken heede vnto my woordes, nor to my Lawe, but cast it off.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 To what purpose bringest thou mee incense from Sheba, and sweete calamus from a farre countrey? Your burnt offerings are not pleasant, nor your sacrifices sweete vnto me.
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 Therefore thus sayeth the Lord, Beholde, I will laie stumbling blockes before this people, and the fathers and the sonnes together shall fall vpon them: the neighbour and his friende shall perish.
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 Thus sayeth the Lord, Beholde, a people commeth from the North countrey, and a great nation shall arise from the sides of the earth.
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 With bowe and shield shall they be weaponed: they are cruell and will haue no compassion: their voyce roareth like the sea, and they ride vpon horses, well appointed, like men of warre against thee, O daughter Zion.
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 We haue heard their fame, and our handes waxe feeble sorrowe is come vpon vs, as the sorrowe of a woman in trauaile.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Goe not foorth into the fielde, nor walke by the way: for the sword of the enemie and feare is on euery side.
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 O daughter of my people, girde thee with sackecloth, and wallowe thy selfe in the ashes: make lamentation, and bitter mourning as for thine onely sonne: for the destroier shall suddenly come vpon vs.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 I haue set thee for a defence and fortresse among my people, that thou maiest knowe and trie their waies.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 They are all rebellious traitours, walking craftily: they are brasse, and yron, they all are destroyers.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 The bellowes are burnt: the lead is consumed in the fire: the founder melteth in vaine: for the wicked are not taken away.
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 They shall call them reprobate siluer, because the Lord hath reiected them.
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< Jeremiah 6 >