< Jeremiah 16 >

1 The worde of the Lord came also vnto mee, saying,
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
2 Thou shalt not take thee a wife, nor haue sonnes nor daughters in this place.
“Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
3 For thus sayeth the Lord concerning the sonnes, and concerning the daughters that are borne in this place, and concerning their mothers that beare them, and concerning their fathers, that beget them in this land,
pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
4 They shall die of deathes and diseases: they shall not be lamented, neither shall they be buried, but they shalbe as dung vpon the earth, and they shalbe consumed by the sword, and by famine, and their carkeises shall be meate for the foules of the heauen, and for the beasts of the earth.
adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
5 For thus saith the Lord, Enter not into the house of mourning, neither goe to lament, nor be moued for the: for I haue taken my peace, from this people, saith the Lord, euen mercy and compassion.
Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
6 Both the great, and the small shall die in this land: they shall not be buried, neither shall men lament for them nor cut themselues, nor make themselues balde for them.
Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
7 They shall not stretch out the hands for the in the mourning to comfort them for the dead, neither shall they giue them the cup of consolation to drinke for their father or for their mother.
Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
8 Thou shalt not also goe into the house of feasting to sit with them to eate and to drinke.
“Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
9 For thus sayth the Lord of hostes, the God of Israel, Beholde, I wil cause to cease out of this place in your eyes, euen in your dayes the voyce of myrth, and the voyce of gladnes, the voyce of the bridegrome and the voyce of the bride.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
10 And when thou shalt shewe this people all these wordes, and they shall say vnto thee, Wherefore hath the Lord pronounced all this great plague against vs? or what is our iniquitie? and what is our sinne that we haue committed against the Lord our God?
“Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
11 Then shalt thou say vnto them, Because your fathers haue forsaken me, sayth the Lord, and haue walked after other gods, and haue serued them, and worshipped them, and haue forsaken me, and haue not kept my Law,
Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
12 (And ye haue done worse then your fathers: for beholde, you walke euery one after the stubbernesse of his wicked heart, and will not heare me)
Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
13 Therefore will I driue you out of this land into a lande that ye knowe not, neither you, nor your fathers, and there shall ye serue other gods day and night: for I will shew you no grace.
Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
14 Behold therfore, saith the Lord, the dayes come that it shall no more be sayde, The Lord liueth, which brought vp the children of Israel out of the land of Egypt,
Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
15 But the Lord liueth, that brought vp the children of Israel from the lande of the North, and from all the landes where hee had scattered them, and I wil bring them againe into their land that I gaue vnto their fathers.
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
16 Behold, sayth the Lord, I wil send out many fishers, and they shall fish them, and after, will I send out many hunters, and they shall hunt them from euery mountaine and from euery hill, and out of the caues of the rockes.
Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
17 For mine eyes are vpon al their wayes: they are not hid from my face, neither is their iniquitie hid from mine eyes.
Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
18 And first I will recompense their iniquitie and their sinne double, because they haue defiled my lande, and haue filled mine inheritance with their filthie carions and their abominations.
Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
19 O Lord, thou art my force, and my strength and my refuge in the day of affliction: the Gentiles shall come vnto thee from the ends of the world, and shall say, Surely our fathers haue inherited lies, and vanitie, wherein was no profite.
Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 Shall a man make gods vnto himselfe, and they are no gods?
Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
21 Beholde, therefore I will this once teach them: I will shewe them mine hande and my power, and they shall know that my Name is the Lord.
“Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.

< Jeremiah 16 >