< Isaiah 59 >

1 Beholde, the Lordes hande is not shortened, that it can not saue: neither is his eare heauie, that it cannot heare.
Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 But your iniquities haue separated betweene you and your God, and your sinnes haue hidde his face from you, that he will not heare.
Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
3 For your handes are defiled with blood, and your fingers with iniquitie: your lips haue spoken lies and your tongue hath murmured iniquitie.
Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 No man calleth for iustice: no man contendeth for trueth: they trust in vanitie, and speake vaine things: they conceiue mischiefe, and bring foorth iniquitie.
Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 They hatch cockatrice egges, and weaue the spiders webbe: he that eateth of their egges, dieth, and that which is trode vpon, breaketh out into a serpent.
Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Their webbes shall be no garment, neither shall they couer themselues with their labours: for their workes are workes of iniquitie, and the worke of crueltie is in their handes.
Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Their feete runne to euill, and they make haste to shed innocent blood: their thoughts are wicked thoughts: desolation and destruction is in their paths.
Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 The way of peace they knowe not, and there is none equitie in their goings: they haue made them crooked paths: whosoeuer goeth therein, shall not knowe peace.
Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Therefore is iudgement farre from vs, neither doeth iustice come neere vnto vs: we waite for light, but loe, it is darkenesse: for brightnesse, but we walke in darkenesse.
Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Wee grope for the wall like the blinde, and we grope as one without eyes: we stumble at the noone day as in the twilight: we are in solitarie places, as dead men.
Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 We roare all like beares, and mourne like dooues: wee looke for equitie, but there is none: for health, but it is farre from vs.
Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 For our trespasses are many before thee, and our sinnes testifie against vs: for our trespasses are with vs, and we knowe our iniquities
Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 In trespassing and lying against the Lord, and wee haue departed away from our God, and haue spoken of crueltie and rebellion, conceiuing and vttering out of the heart false matters.
Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Therefore iudgement is turned backewarde, and iustice standeth farre off: for trueth is fallen in the streete, and equitie cannot enter.
Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Yea, trueth faileth, and hee that refraineth from euill, maketh himselfe a praye: and when the Lord sawe it, it displeased him, that there was no iudgement.
Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 And when he sawe that there was no man, hee wondered that none woulde offer him selfe. Therefore his arme did saue it, and his righteousnes it selfe did sustaine it.
Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 For he put on righteousnes, as an habergeon, and an helmet of saluation vpon his head, and he put on the garments of vengeance for clothing, and was clad with zeale as a cloke.
Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 As to make recompence, as to requite the furie of the aduersaries with a recompence to his enemies: he will fully repaire the ylands.
Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 So shall they feare the Name of the Lord from the West, and his glory from the rising of the sunne: for the enemie shall come like a flood: but the Spirit of the Lord shall chase him away.
Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 And the Redeemer shall come vnto Zion, and vnto them that turne from iniquitie in Iaakob, saith the Lord.
“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
21 And I will make this my couenant with them, saith the Lord. My Spirit that is vpon thee, and my wordes, which I haue put in thy mouth, shall not depart out of thy mouth, nor out of the mouth of thy seede, nor out of the mouth of the seede of thy seede, saith the Lord, from hencefoorth euen for euer.
Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.

< Isaiah 59 >