< Isaiah 51 >

1 Heare me, ye that follow after righteousnes, and ye that seeke the Lord: looke vnto the rocke, whence ye are hewen, and to the hole of the pit, whence ye are digged.
“Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
2 Consider Abraham your father, and Sarah that bare you: for I called him alone, and blessed him, and increased him.
taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
3 Surely the Lord shall comfort Zion: he shall comfort all her desolations, and he shall make her desert like Eden, and her wildernes like the garden of the Lord: ioy and gladnesse shalbe founde therein: praise, and the voyce of singing.
Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
4 Hearken ye vnto me, my people, and giue eare vnto me, O my people: for a Law shall proceede from me, and I will bring foorth my iudgement for the light of the people.
“Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
5 My righteousnes is neere: my saluation goeth foorth, and mine armes shall iudge the people: the yles shall waite for me, and shall trust vnto mine arme.
Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
6 Lift vp your eyes to the heauens, and looke vpon the earth beneath: for the heauens shall vanish away like smoke, and the earth shall waxe olde like a garment, and they that dwell therein, shall perish in like maner: but my saluation shall be for euer, and my righteousnesse shall not bee abolished.
Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
7 Hearken vnto me, ye that know righteousnesse, the people in whose heart is my Lawe. Feare ye not the reproche of men, neither be ye afraide of their rebukes.
“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
8 For the mothe shall eate them vp like a garment, and the worme shall eate them like wool: but my righteousnesse shalbe for euer, and my saluation from generation to generation.
Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
9 Rise vp, rise vp, and put on strength, O arme of the Lord: rise vp as in the olde time in the generations of the worlde. Art not thou the same, that hath cutte Rahab, and wounded the dragon?
Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Art not thou the same, which hath dried the Sea, euen the waters of the great deepe, making the depth of the Sea a way for the redeemed to passe ouer?
Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Therefore the redeemed of the Lord shall returne, and come with ioy vnto Zion, and euerlasting ioy shalbe vpon their head: they shall obtaine ioy, and gladnesse: and sorow and mourning shall flee away.
Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
12 I, euen I am he, that comfort you. Who art thou, that thou shouldest feare a mortall man, and the sonne of man, which shalbe made as grasse?
Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 And forgettest the Lord thy maker, that hath spred out the heauens, and layde the foundations of the earth? and hast feared continually all the day, because of the rage of the oppressour, which is readie to destroy? Where is now the rage of the oppressour?
Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14 The captiue hasteneth to be loosed, and that hee should not die in the pitte, nor that his bread should faile.
Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
15 And I am the Lord thy God that deuided the Sea, when his waues roared: the Lord of hostes is his Name.
Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 And I haue put my wordes in thy mouth, and haue defended thee in the shadowe of mine hand, that I may plant the heauens, and lay the foundation of the earth, and say vnto Zion, Thou art my people.
Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
17 Awake, awake, and stande vp, O Ierusalem, which hast drunke at the hande of the Lord the cup of his wrath: thou hast drunken the dregges of the cup of trembling, and wrung them out.
Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
18 There is none to guide her among all the sonnes, whome she hath brought foorth: there is none that taketh her by the hand of all the sonnes that she hath brought vp.
Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
19 These two thinges are come vnto thee: who will lament thee? desolation and destruction and famine, and the sworde: by whome shall I comfort thee?
Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
20 Thy sonnes haue fainted, and lye at the head of all the streetes as a wilde bull in a nette, and are full of the wrath of the Lord, and rebuke of thy God.
Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
21 Therefore heare nowe this, thou miserable and drunken, but not with wine.
Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
22 Thus saith thy Lord God, euen God that pleadeth the cause of his people, Beholde, I haue taken out of thine hande the cuppe of trembling, euen the dregges of the cuppe of my wrath: thou shalt drinke it no more.
Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
23 But I will put it into their hande that spoile thee: which haue said to thy soule, Bowe downe, that wee may goe ouer, and thou hast layde thy bodie as the grounde, and as the streete to them that went ouer.
Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”

< Isaiah 51 >