< Isaiah 24 >

1 Behold, the Lord maketh the earth emptie, and hee maketh it waste: hee turneth it vpside downe, and scattereth abrode the inhabitants thereof.
Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
2 And there shalbe like people, like Priest, and like seruaunt, like master, like maide, like mistresse, like bier, like seller, like lender, like borower, like giuer, like taker to vsurie.
Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
3 The earth shalbe cleane emptied, and vtterly spoiled: for the Lord hath spoken this worde.
Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
4 The earth lamenteth and fadeth away: the world is feeble and decaied: the proude people of the earth are weakened.
Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
5 The earth also deceiueth, because of the inhabitantes thereof: for they transgressed the lawes: they changed the ordinances, and brake the euerlasting couenant.
Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
6 Therefore hath the curse deuoured the earth, and the inhabitantes thereof are desolate. Wherefore the inhabitants of the land are burned vp, and fewe men are left.
Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
7 The wine faileth, the vine hath no might: all that were of merie heart, doe mourne.
Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
8 The mirth of tabrets ceaseth: the noyse of them that reioyce, endeth: the ioye of the harpe ceaseth.
Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
9 They shall not drinke wine with mirth: strong drinke shall be bitter to them that drinke it.
Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10 The citie of vanitie is broken downe: euery house is shut vp, that no man may come in.
Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
11 There is a crying for wine in the streetes: al ioy is darkened: the mirth of the world is gone away.
Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12 In the citie is left desolation, and the gate is smitten with destruction.
Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
13 Surely thus shall it bee in the middes of the earth, among the people, as the shaking of an oliue tree, and as the grapes when the vintage is ended.
Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
14 They shall lift vp their voyce: they shall shout for the magnificence of the Lord: they shall reioyce from the sea.
Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15 Wherefore praise yee the Lord in the valleis, euen the Name of the Lord God of Israel, in the yles of the sea.
Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16 From the vttermost part of the earth wee haue heard praises, euen glory to the iust, and I sayd, My leanesse, my leanesse, woe is mee: the transgressours haue offended: yea, the transgressours haue grieuously offended.
Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
17 Feare, and the pitte, and the snare are vpon thee, O inhabitant of the earth.
Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
18 And hee that fleeth from the noyse of the feare, shall fall into the pit: and he that commeth vp out of the pit, shall be taken in the snare: for the windowes from on high are open, and the foundations of the earth doe shake.
Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
19 The earth is vtterly broken downe: the earth is cleane dissolued: the earth is mooued exceedingly.
Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
20 The earth shall reele to and from like a drunken man, and shall be remooued like a tent, and the iniquitie thereof shall be heauie vpon it: so that it shall fall, and rise no more.
Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
21 And in that day shall the Lord visite the hoste aboue that is on hie, euen the Kinges of the world that are vpon the earth.
Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
22 And they shall be gathered together, as the prisoners in the pit: and they shall be shut vp in the prison, and after many daies shall they be visited.
Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
23 Then the moone shall be abashed, and the sunne ashamed, when the Lord of hostes shall reigne in mount Zion and in Ierusalem: and glory shalbe before his ancient men.
Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.

< Isaiah 24 >