< Isaiah 21 >

1 The burden of the desert Sea. As the whirlewindes in the South vse to passe from the wildernesse, so shall it come from the horrible land.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 A grieuous vision was shewed vnto me, The transgressour against a transgressour, and the destroyer against a destroyer. Goe vp Elam, besiege Media: I haue caused all the mourning thereof to cease.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Therefore are my loynes filled with sorow: sorowes haue taken me as the sorowes of a woman that trauayleth: I was bowed downe when I heard it, and I was amased when I sawe it.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Mine heart failed: fearefulnesse troubled me: the night of my pleasures hath he turned into feare vnto me.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Prepare thou the table: watch in the watch towre: eate, drinke: arise, ye princes, anoynt the shielde.
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 For thus hath the Lord said vnto me, Go, set a watchman, to tell what he seeth.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 And he sawe a charet with two horsemen: a charet of an asse, and a charet of a camel: and he hearkened and tooke diligent heede.
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 And he cryed, A lyon: my lorde, I stand continually vpon ye watche towre in the day time, and I am set in my watche euery night:
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 And beholde, this mans charet commeth with two horsemen. And he answered and said, Babel is fallen: it is fallen, and all the images of her gods hath he broken vnto the ground.
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 O my threshing, and the corne of my floore. That which I haue heard of the Lord of hostes, the God of Israel, haue I shewed vnto you.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 The burden of Dumah. He calleth vnto me out of Seir, Watchman, what was in ye night? Watchman, what was in the night?
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 The watchman saide, The morning commeth, and also the night. If yee will aske, enquire: returne and come.
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 The burden against Arabia. In the forest of Arabia shall yee tarie all night, euen in the waies of Dedanim.
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 O inhabitants of the lande of Tema, bring foorth water to meete the thirstie, and preuent him that fleeth with his bread.
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 For they flee from the drawen swords, euen from the drawen sword, and from the bent bowe, and from the grieuousnesse of warre.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 For thus hath the Lord sayd vnto me, Yet a yeere according to the yeeres of an hireling, and all the glorie of Kedar shall faile.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 And the residue of the nomber of ye strong archers of the sonnes of Kedar shall be fewe: for the Lord God of Israel hath spoken it.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

< Isaiah 21 >