< Hosea 7 >

1 When I woulde haue healed Israel, then the iniquitie of Ephraim was discouered, and the wickednesse of Samaria: for they haue dealt falsly: and the theefe commeth in, and the robber spoyleth without.
Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
2 And they consider not in their hearts, that I remember all their wickednes: now their owne inuentions haue beset them about: they are in my sight.
Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
3 They make the King glad with their wickednesse, and the princes with their lies.
“Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
4 They are all adulterers, and as a very ouen heated by ye baker, which ceaseth from raysing vp, and from kneading ye dough vntill it be leauened.
Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
5 This is the day of our King: the princes haue made him sicke with flagons of wine: he stretcheth out his hand to scorners.
Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
6 For they haue made ready their heart like an ouen whiles they lie in waite: their baker sleepeth all the night: in the morning it burneth as a flame of fire.
Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
7 They are all hote as an ouen, and haue deuoured their iudges: all their Kings are fallen: there is none among them that calleth vnto me.
Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
8 Ephraim hath mixt himselfe among the people. Ephraim is as a cake on the hearth not turned.
“Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
9 Strangers haue deuoured his strength, and he knoweth it not: yea, gray heares are here and there vpon him, yet he knoweth not.
Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
10 And the pride of Israel testifieth to his face, and they doe not returne to the Lord their God, nor seeke him for all this.
Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
11 Ephraim also is like a doue deceiued, without heart: they call to Egypt: they go to Asshur.
“Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
12 But when they shall go, I will spred my net vpon them, and drawe them downe as the foules of the heauen: I will chastice them as their congregation hath heard.
Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
13 Wo vnto them: for they haue fled away from me: destruction shalbe vnto them, because they haue transgressed against me: though I haue redeemed them, yet they haue spoken lyes against me.
Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
14 And they haue not cryed vnto me with their hearts, when they houled vpon their beds: they assembled themselues for corne, and wine, and they rebell against me.
Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
15 Though I haue boud and strengthened their arme, yet doe they imagine mischiefe against me.
Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
16 They returne, but not to the most high: they are like a deceitfull bowe: their princes shall fall by the sword, for the rage of their tongues: this shall be their derision in the land of Egypt.
Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.

< Hosea 7 >