< Genesis 49 >

1 Then Iaakob called his sonnes, and sayde, Gather your selues together, that I may tell you what shall come to you in the last dayes.
Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
2 Gather your selues together, and heare, ye sonnes of Iaakob, and hearken vnto Israel your father.
“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
3 Reuben mine eldest sonne, thou art my might, and the beginning of my strength, the excellencie of dignitie, and the excellencie of power:
“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
4 Thou wast light as water: thou shalt not be excellent, because thou wentest vp to thy fathers bed: then diddest thou defile my bed, thy dignitie is gone.
Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
5 Simeon and Leui, brethren in euill, the instruments of crueltie are in their habitations.
“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
6 Into their secret let not my soule come: my glory, be not thou ioyned with their assembly: for in their wrath they slew a man, and in their selfe will they digged downe a wall.
Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
7 Cursed be their wrath, for it was fierce, and their rage, for it was cruell: I will deuide them in Iaakob, and scatter them in Israel.
Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
8 Thou Iudah, thy brethre shall praise thee: thine hande shalbe in the necke of thine enemies: thy fathers sonnes shall bowe downe vnto thee.
“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
9 Iudah, as a Lions whelpe shalt thou come vp from the spoyle, my sonne. He shall lye downe and couche as a Lion, and as a Lionesse: Who shall stirre him vp?
Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
10 The scepter shall not depart from Iudah, nor a Lawegiuer from betweene his feete, vntill Shiloh come, and the people shall be gathered vnto him.
Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
11 He shall binde his Asse foale vnto ye vine, and his Asses colte vnto the best vine. hee shall wash his garment in wine, and his cloke in the blood of grapes.
Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
12 His eyes shalbe red with wine, and his teeth white with milke.
Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
13 Zebulun shall dwell by the sea side, and he shalbe an hauen for shippes: and his border shalbe vnto Zidon.
“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
14 Issachar shalbe a strong asse, couching downe betweene two burdens:
“Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
15 And he shall see that rest is good, and that the land is pleasant, and he shall bow his shoulder to beare, and shalbe subiect vnto tribute.
Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
16 Dan shall iudge his people as one of the tribes of Israel.
“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
17 Dan shall be a serpent by the way, an adder by the path, byting the horse heeles, so that his rider shall fall backward.
Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
18 O Lord, I haue waited for thy saluation.
“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
19 Gad, an hoste of men shall ouercome him, but he shall ouercome at the last.
“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
20 Concerning Asher, his bread shalbe fat, and he shall giue pleasures for a king.
“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
21 Naphtali shalbe a hinde let goe, giuing goodly wordes.
“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
22 Ioseph shalbe a fruitefull bough, euen a fruitful bough by the well side: the small boughs shall runne vpon the wall.
“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
23 And the archers grieued him, and shotte against him and hated him.
Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
24 But his bowe abode strong, and the hands of his armes were strengthened, by the handes of the mighty God of Iaakob, of whom was the feeder appointed, by the stone of Israel,
Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
25 Euen by the God of thy father, who shall helpe thee, and by the almightie, who shall blesse thee with heauenly blessinges from aboue, with blessings of the deepe, that lyeth beneath, with blessings of the brestes, and of the wombe.
Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
26 The blessings of thy father shalbe stronger then the blessings of mine elders: vnto the ende of the hilles of the worlde they shall be on the head of Ioseph, and on the top of the head of him that was separate from his brethren.
Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
27 Beniamin shall rauine as a wolfe: in the morning he shall deuoure the pray, and at night he shall deuide the spoyle.
“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
28 All these are the twelue tribes of Israel, and thus their father spake vnto them, and blessed them: euery one of them blessed hee with a seuerall blessing.
Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
29 And he charged them and sayd vnto them, I am ready to be gathered vnto my people: burie mee with my fathers in the caue, that is in the fielde of Ephron the Hittite,
Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
30 In the caue that is in the field of Machpelah besides Mamre in the land of Canaan: which caue Abraham bought with the fielde of Ephron the Hittite for a possession to burie in.
Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
31 There they buried Abraham and Sarah his wife: there they buryed Izhak and Rebekah his wife: and there I buried Leah.
Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
32 The purchase of the fielde and the caue that is therein, was bought of the children of Heth.
Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
33 Thus Iaakob made an end of giuing charge to his sonnes, and plucked vp his feete into the bed and gaue vp the ghost, and was gathered to his people.
Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

< Genesis 49 >