< Genesis 10 >

1 Now these are the generations of the sonnes of Noah, Shem, Ham and Iapheth: vnto whom sonnes were borne after the flood.
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 The sonnes of Iapheth were Gomer and Magog, and Madai, and Iauan, and Tubal, and Meshech, and Tiras.
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 And the sonnes of Gomer, Ashkenaz, and Riphath, and Togarmah.
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 Also the sonnes of Iauan, Elishah and Tarshish, Kittim, and Dodanim.
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 Of these were the yles of the Gentiles deuided in their landes, euery man after his tongue, and after their families in their nations.
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 Moreouer, ye sonnes of Ham were Cush, and Mizraim, and Put, and Canaan.
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 And the sonnes of Cush, Seba and Hauilah, and Sabtah, and Raamah, and Sabtecha: also the sonnes of Raamah were Sheba and Dedan.
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 And Cush begate Nimrod, who began to be mightie in the earth.
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 He was a mightie hunter before the Lord. wherefore it is saide, As Nimrod the mightie hunter before the Lord.
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 And the beginning of his kingdome was Babel, and Erech, and Accad, and Calneh, in the land of Shinar.
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 Out of that land came Asshur, and builded Niniueh, and the citie Rehoboth, and Calah:
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 Resen also betweene Niniueh and Calah: this is a great citie.
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 And Mizraim begate Ludim, and Anamim, and Lehabim, and Naphtuhim.
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 Pathrusim also, and Casluhim (out of whom came the Philistims) and Caphtorims.
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 Also Canaan begat Zidon his first borne, and Heth,
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 And Iebusi, and Emori, and Girgashi,
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 And Hiui, and Arki, and Sini,
Ahivi, Aariki, Asini,
18 And Aruadi, and Zemari, and Hamathi: and afterwarde were the families of the Canaanites spred abroade.
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 Then the border of the Canaanites was from Zidon, as thou commest to Gerar vntil Azzah, and as thou goest vnto Sodom, and Gomorah, and Admah, and Zeboijm, euen vnto Lasha.
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 These are the sonnes of Ham according to their families, according to their tongues in their countries and in their nations.
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 Vnto Shem also the father of all the sonnes of Eber, and elder brother of Iapheth were children borne.
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 The sonnes of Shem were Elam and Asshur, and Arpachshad, and Lud, and Aram.
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 And the sonnes of Aram, Vz and Hul, and Gether and Mash.
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 Also Arpachshad begate Shelah, and Shelah begate Eber.
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 Vnto Eber also were borne two sonnes: the name of the one was Peleg: for in his dayes was the earth diuided: and his brothers name was Ioktan.
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 Then Ioktan begate Almodad and Sheleph, and Hazarmaueth, and Ierah,
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 And Hadoram, and Vzal, and Dicklah,
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 And Obal, and Abimael, and Sheba,
Obali, Abimaeli, Seba,
29 And Ophir, and Hauilah, and Iobab: all these were the sonnes of Ioktan.
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 And their dwelling was from Mesha, as thou goest vnto Sephar a mount of the East.
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 These are the sonnes of Shem according to their families, according to their tongues, in their countreis and nations.
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 These are the families of the sonnes of Noah, after their generations among their people: and out of these were the nations diuided in the earth after the flood.
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< Genesis 10 >