+ Genesis 1 >

1 In the beginning God created the heauen and the earth.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 And the earth was without forme and void, and darkenesse was vpon the deepe, and the Spirit of God mooued vpon the waters.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 Then God said, Let there be light: And there was light.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 And God saw the light that it was good, and God separated the light from the darkenes.
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 And God called the Light, Day, and the darkenes, he called Night. So the euening and the morning were the first day.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 Againe God said, Let there be a firmament in the mids of the waters: and let it separate the waters from the waters.
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 Then God made the firmament, and separated the waters, which were vnder the firmament, from the waters which were aboue the firmament: and it was so.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 And God called the firmament Heauen. So the Euening and the morning were the second day.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 God said againe, Let the waters vnder the heauen be gathered into one place, and let the dry land appeare. and it was so.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 And God called the dry land, Earth, and he called the gathering together of the waters, Seas: and God saw that it was good.
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 Then God said, Let the earth bud forth the bud of the herbe, that seedeth seed, the fruitfull tree, which beareth fruite according to his kinde, which hath his seede in it selfe vpon the earth: and it was so.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 And the earth brought foorth the bud of the herbe, that seedeth seede according to his kind, also the tree that beareth fruit, which hath his seed in it selfe according to his kinde: and God saw that it was good.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 So the euening and the morning were the third day.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 And God said, Let there be lights in the firmament of the heauen, to separate the day from the night, and let them be for signes, and for seasons, and for dayes and yeeres.
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 And let them be for lights in the firmament of the heauen to giue light vpon the earth: and it was so.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 God then made two great lights: the greater light to rule the day, and the lesse light to rule the night: he made also the starres.
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 And God set them in the firmament of the heauen, to shine vpon the earth,
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 And to rule in the day, and in the night, and to separate the light from the darkenesse: and God saw that it was good.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 So the euening and the morning were the fourth day.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 Afterward God said, Let the waters bring foorth in abundance euery creeping thing that hath life: and let the foule flie vpon the earth in the open firmament of the heauen.
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 Then God created the great whales, and euery thing liuing and mouing, which the waters brought foorth in abundance according to their kinde, and euery fethered foule according to his kinde: and God sawe that it was good.
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 Then God blessed them, saying, Bring foorth fruite and multiplie, and fill the waters in the seas, and let the foule multiplie in the earth.
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 So the euening and the morning were the fifte day.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 Moreouer God said, Let the earth bring foorth the liuing thing according to his kinde, cattel, and that which creepeth, and the beast of the earth, according to his kinde. and it was so.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 And God made the beast of the earth according to his kinde, and the cattell according to his kinde, and euery creeping thing of the earth according to his kind: and God saw that it was good.
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 Furthermore God said, Let vs make man in our image according to our likenes, and let them rule ouer the fish of the sea, and ouer the foule of the heauen, and ouer the beastes, and ouer all the earth, and ouer euery thing that creepeth and moueth on the earth.
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 Thus God created the man in his image: in the image of God created he him: he created them male and female.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 And God blessed them, and God said to them, Bring forth fruite and multiplie, and fill the earth, and subdue it, and rule ouer the fish of the sea, and ouer the foule of the heauen, and ouer euery beast that moueth vpon the earth.
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 And God said, Beholde, I haue giuen vnto you euery herbe bearing seede, which is vpon al the earth, and euery tree, wherein is the fruite of a tree bearing seede: that shall be to you for meate.
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 Likewise to euery beast of the earth, and to euery foule of the heauen, and to euery thing that moueth vpon the earth, which hath life in it selfe, euery greene herbe shall be for meate. and it was so.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 And God sawe all that he had made, and loe, it was very good. So the euening and the morning were the sixt day.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

+ Genesis 1 >