< Ezekiel 5 >

1 And thou sonne of man, take thee a sharpe knife, or take thee a barbours rasor and cause it to passe vpon thine head, and vpon thy beard: then take thee balances to weigh, and deuide the heare.
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 Thou shalt burne with fire the thirde part in the middes of the citie, when the dayes of the siege are fulfilled, and thou shalt take the other thirde part, and smite about it with a knife, and the last thirde part thou shalt scatter in the winde, and I will drawe out a sworde after them.
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 Thou shalt also take thereof a fewe in nomber, and binde them in thy lappe.
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 Then take of them againe and cast them into the middes of the fire, and burne them in the fire: for thereof shall a fire come foorth into all the house of Israel.
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 Thus saith the Lord God, This is Ierusalem: I haue set it in the middes of the nations and countreyes, that are rounde about her.
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 And she hath changed my iudgements into wickednes more then the nations, and my statutes more then the countreis, that are round about her: for they haue refused my iudgemets and my statutes, and they haue not walked in them.
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 Therefore thus saith the Lord God, Because your multitude is greater then the nations that are rounde about you, and ye haue not walked in my statutes, neither haue ye kept my iudgements: no, ye haue not done according to the iudgements of the nations, that are rounde about you,
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 Therefore thus saith the Lord God, Beholde, I, euen I come against thee, and will execute iudgement in the middes of thee, euen in the sight of the nations.
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 And I will doe in thee, that I neuer did before, neither will do any more the like, because of all thine abominations.
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 For in the middes of thee, the fathers shall eate their sonnes, and the sonnes shall eate their fathers, and I will execute iudgement in thee, and the whole remnant of thee will I scatter into all the windes.
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 Wherefore, as I liue, saith the Lord God, Surely because thou hast defiled my Sanctuarie with all thy filthinesse, and with all thine abominations, therefore will I also destroy thee, neither shall mine eye spare thee, neither will I haue any pitie.
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 The third part of thee shall die with the pestilence, and with famine shall they bee consumed in the middes of thee: and another third part shall fall by the sword round about thee: and I will scatter the last third part into all windes, and I will drawe out a sword after them.
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 Thus shall mine anger bee accomplished, and I will cause my wrath to cease in them, and I will be comforted: and they shall knowe, that I the Lord haue spoke it in my zeale, when I haue accomplished my wrath in them.
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 Moreouer, I will make thee waste, and abhorred among the nations, that are round about thee, and in the sight of all that passe by.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 So thou shalt bee a reproche and shame, a chastisement and an astonishment vnto the nations, that are rounde about thee, when I shall execute iudgements in thee, in anger and in wrath, and in sharpe rebukes: I the Lord haue spoken it.
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 When I shall sende vpon them the euill arrowes of famine, which shalbe for their destruction, and which I will sende to destroy you: and I will encrease the famine vpon you, and wil breake your staffe of bread.
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 So will I send vpon you famine, and euill beastes, and they shall spoyle thee, and pestilence and blood shall passe through thee, and I will bring the sworde vpon thee: I the Lord haue spoken it.
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< Ezekiel 5 >