< Ecclesiastes 12 >

1 Remember nowe thy Creator in the daies of thy youth, whiles the euill daies come not, nor the yeeres approche, wherein thou shalt say, I haue no pleasure in them:
Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
2 Whiles the sunne is not darke, nor ye light, nor the moone, nor the starres, nor the cloudes returne after the raine:
Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
3 When the keepers of ye house shall tremble, and the strong men shall bow them selues, and the grinders shall cease, because they are few, and they waxe darke that looke out by ye windowes:
Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
4 And the doores shall be shut without by the base sound of the grinding, and he shall rise vp at the voice of the birde: and all the daughters of singing shall be abased.
Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
5 Also they shalbe afraide of the hie thing, and feare shalbe in the way, and the almond tree shall flourish, and the grassehopper shall be a burden, and concupiscence shall be driuen away: for man goeth to the house of his age, and the mourners goe about in the streete.
Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
6 Whiles the siluer coarde is not lengthened, nor the golden ewer broken, nor the pitcher broken at the well, nor the wheele broken at the cisterne:
Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
7 And dust returne to the earth as it was, and the spirit returne to God that gaue it.
Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
8 Vanitie of vanities, saieth the Preacher, all is vanitie.
“Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
9 And the more wise the Preacher was, the more he taught the people knowledge, and caused them to heare, and searched foorth, and prepared many parables.
Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
10 The Preacher sought to finde out pleasant wordes, and an vpright writing, euen the wordes of trueth.
Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
11 The wordes of the wise are like goads, and like nailes fastened by the masters of the assemblies, which are giuen by one pastour.
Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
12 And of other things beside these, my sone, take thou heede: for there is none ende in making many bookes, and much reading is a wearines of the flesh.
Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
13 Let vs heare the end of all: feare God and keepe his commandements: for this is the whole duetie of man.
Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
14 For God will bring euery worke vnto iudgement, with euery secret thing, whether it be good or euill.
Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.

< Ecclesiastes 12 >