< Amos 3 >

1 Heare this worde that the Lord pronounceth against you, O children of Israel, euen against the whole familie which I brought vp from the land of Egypt, saying,
Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2 You onely haue I knowen of all the families of the earth: therefore I will visite you for all your iniquities.
“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
3 Can two walke together except they bee agreed?
Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
4 Will a lion roare in ye forest, when he hath no pray? or wil a lions whelpe cry out of his den, if he haue taken nothing?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
5 Can a birde fall in a snare vpon the earth, where no fouler is? or will he take vp the snare from the earth, and haue taken nothing at all?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
6 Or shall a trumpet be blowen in the citie, and the people be not afraide? or shall there be euil in a citie, and the Lord hath not done it?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7 Surely the Lord God will doe nothing, but he reueileth his secrete vnto his seruantes the Prophets.
Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
8 The lyon hath roared: who will not bee afraide? the Lord God hath spoken: who can but prophecie?
Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
9 Proclayme in the palaces at Ashdod, and in the palaces in the lande of Egypt, and saye, Assemble your selues vpon the mountaines of Samaria: so beholde the great tumultes in the middes thereof, and the oppressed in the middes thereof.
Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10 For they knowe not to doe right, sayth the Lord: they store vp violence, and robbery in their palaces.
“Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11 Therefore thus saith the Lord God, An aduersary shall come euen rounde about the countrey, and shall bring downe thy strength from thee, and thy palaces shalbe spoyled.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12 Thus saieth the Lord, As the shephearde taketh out of the mouth of the lyon two legges, or a piece of an eare: so shall the children of Israel be taken out that dwell in Samaria in the corner of a bed, and in Damascus, as in a couche.
Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13 Heare, and testifie in the house of Iaakob, saith the Lord God, the God of hostes.
“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14 Surely in the day that I shall visit the transgressions of Israel vpon him, I wil also visite the altars of Beth-el, and the hornes of the altar shall be broken off, and fall to the ground.
“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
15 And I wil smite the winter house with the sommer house, and the houses of yuorie shall perish, and the great houses shalbe consumed, sayth the Lord.
Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.

< Amos 3 >