< 2 Samuel 1 >

1 After the death of Saul, when Dauid was returned from the slaughter of the Amalekites and had beene two dayes in Ziklag,
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 Behold, a man came the third day out of the host from Saul with his clothes rent, and earth vpon his head: and when hee came to Dauid, he fell to the earth, and did obeisance.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 Then Dauid saide vnto him, Whence commest thou? And he said vnto him, Out of the host of Israel I am escaped.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 And Dauid saide vnto him, What is done? I pray thee, tell me. Then he said, that the people is fled from the battel, and many of the people are ouerthrowen, and dead, and also Saul and Ionathan his sonne are dead.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 And Dauid saide vnto the yong man that tolde it him, Howe knowest thou that Saul and Ionathan his sonne be dead?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 Then the yong man that tolde him, answered, As I came to mount Gilboa, behold, Saul leaned vpon his speare, and loe, the charets and horsemen followed hard after him.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 And when he looked backe, he saw me, and called me. And I answered, Here am I.
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 And he said vnto me, Who art thou? And I answered him, I am an Amalekite.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 Then saide hee vnto me, I pray thee come vpon mee, and slay me: for anguish is come vpon me, because my life is yet whole in me.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 So I came vpon him, and slewe him, and because I was sure that hee coulde not liue, after that hee had fallen, I tooke the crowne that was vpon his head, and the bracelet that was on his arme, and brought them hither vnto my lord.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Then Dauid tooke hold on his clothes, and rent them, and likewise al the men that were with him.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 And they mourned and wept, and fasted vntil euen, for Saul and for Ionathan his sonne, and for the people of the Lord, and for the house of Israel, because they were slaine with the sword.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 Afterward Dauid saide vnto the yong man that tolde it him, Whence art thou? And hee answered, I am the sonne of a stranger an Amalekite.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 And Dauid said vnto him, How wast thou not afrayd, to put forth thine hand to destroy the Anoynted of the Lord?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 Then Dauid called one of his yong men, and said, Goe neere, and fall vpon him. And hee smote him that he dyed.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 Then said Dauid vnto him, Thy blood be vpon thine owne head: for thine owne mouth hath testified against thee, saying, I haue slaine the Lords Anoynted.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Then Dauid mourned with this lamentation ouer Saul, and ouer Ionathan his sonne,
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 (Also he bade them teach the children of Iudah to shoote, as it is written in the booke of Iasher)
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 O noble Israel, hee is slane vpon thy hie places: how are the mightie ouerthrowen!
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Tell it not in Gath, nor publish it in the streetes of Ashkelon, lest the daughters of the Philistims reioyce, lest the daughters of the vncircumcised triumph.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 Ye mountaines of Gilboa, vpon you be neither dewe nor raine, nor be there fieldes of offrings: for there the shielde of the mightie is cast downe, the shielde of Saul, as though he had not bene anointed with oyle.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 The bow of Ionathan neuer turned backe, neither did the sword of Saul returne emptie from the blood of the slaine, and from the fatte of the mightie.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saul and Ionathan were louely and pleasant in their liues, and in their deaths they were not deuided: they were swifter then eagles, they were stronger then lions.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 Yee daughters of Israel, weepe for Saul, which clothed you in skarlet, with pleasures, and hanged ornaments of gold vpon your apparel.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Howe were the mightie slaine in the mids of the battel! O Ionathan, thou wast slaine in thine hie places.
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Wo is me for thee, my brother Ionathan: very kinde hast thou bene vnto me: thy loue to me was wonderfull, passing the loue of women:
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 howe are the mightie ouerthrowen, and the weapons of warre destroyed!
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuel 1 >